< Masalimo 37 >
1 Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
Af David. Lad din Vrede ikke optændes imod de onde; vær ikke nidkær imod dem, som gøre Uret;
2 pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
thi de skulle hastelig falme som Græs, og visne som grønne Urter.
3 Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
Forlad dig paa Herren og gør godt; bo i Landet og nær dig trolig;
4 Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
og forlyst dig i Herren, saa skal han give dig dit Hjertes Begæring.
5 Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
Vælt din Vej paa Herren og forlad dig paa ham, han skal gøre det.
6 Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
Og han skal føre din Retfærdighed frem som Lyset og din Ret som Middagsglansen.
7 Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
Ti for Herren og forvent ham; lad din Vrede ikke optændes imod den Mand, hvis Vej lykkes, imod den Mand, som øver Underfundighed.
8 Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
Lad af fra Vrede og lad Heftighed fare, lad din Vrede ikke optændes, den er kun til at gøre ondt.
9 Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
Thi de onde skulle udryddes, men de, som bie efter Herren, de skulle arve Landet.
10 Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
Og endnu et lidet, saa er den ugudelige ikke mere; og naar du giver Agt paa hans Sted, da er han borte.
11 Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
Men de sagtmodige skulle arve Landet og forlyste sig over stor Fred.
12 Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
Den ugudelige optænker Skalkhed imod den retfærdige og skærer Tænder imod ham.
13 koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
Herren skal le ad ham; thi han ser, at hans Dag er kommen.
14 Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
De ugudelige have uddraget Sværd og spændt deres Bue at fælde en elendig og fattig, at tage Livet af dem, som vandre i Oprigtighed.
15 Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
Deres Sværd skal komme i deres eget Hjerte, og deres Buer skulle sønderbrydes.
16 Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
Det lidet, som den retfærdige har, er bedre end mange ugudeliges Gods.
17 pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
Thi de ugudeliges Arme skulle sønderbrydes; men Herren opholder de retfærdige.
18 Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
Herren kender de retsindiges Dage, og deres Arv skal blive evindelig.
19 Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
De skulle ikke beskæmmes i den onde Tid, og de skulle mættes i Hungers Dage.
20 Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
Thi de ugudelige skulle omkomme, ja, Herrens Fjender, som Engenes Pragt; de ere forsvundne, i Røg forsvundne.
21 Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
En ugudelig maa tage til Laans, og kan ikke betale; men en retfærdig kan forbarme sig og giver.
22 Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
Thi Herrens velsignede skulle arve Landet; men hans forbandede skulle udryddes.
23 Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
Af Herren stadfæstes en Mands Gang, og han vil have Velbehag til hans Vej.
24 ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
Naar han falder, bliver han ikke liggende; thi Herren holder fast ved hans Haand.
25 Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
Jeg har været ung og er bleven gammel; men jeg har ikke set en retfærdig forladt eller hans Sæd at søge efter Brødet.
26 Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
Han forbarmer sig den ganske Dag og laaner ud, og hans Sæd skal blive til en Velsignelse.
27 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
Vig fra ondt, og gør godt, saa skal du blive boende evindelig.
28 Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
Thi Herren elsker Ret og forlader ikke sine hellige, de ere bevarede evindelig; men de ugudeliges Sæd er udryddet.
29 olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
De retfærdige skulle arve Landet og bo der evindelig.
30 Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
En retfærdigs Mund skal tale Visdom, og hans Tunge skal forkynde Ret.
31 Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
Hans Guds Lov er i hans Hjerte; hans Trin skulle ikke glide.
32 Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
En ugudelig lurer paa den retfærdige og søger efter at dræbe ham.
33 koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
Herren skal ikke overlade ham i hans Haand og ej kende ham skyldig, naar han dømmes.
34 Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
Bi efter Herren og var paa hans Vej, saa skal han ophøje dig til at arve Landet; du skal se paa de ugudeliges Udryddelse.
35 Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
Jeg saa en ugudelig, en Voldsmand; han udbredte sig som et grønt Rodskud.
36 Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
Men han forsvandt og se, han var ikke mere; og jeg søgte efter ham, men han fandtes ikke.
37 Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
Tag Vare paa den retsindige, og se hen til den oprigtige, thi Fredens Mand har en Fremtid.
38 Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
Men Overtrædere skulle ødelægges til Hobe; de ugudeliges Fremtid er borte.
39 Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
Men de retfærdiges Frelse er af Herren, han er deres Styrke i Nødens Tid.
40 Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.
Og Herren skal hjælpe dem og udfri dem; han skal udfri dem fra de ugudelige og frelse dem; thi de have forladt sig paa ham.