< Masalimo 36 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova. Uthenga uli mu mtima mwanga wonena za kuchimwa kwa munthu woyipa: Mu mtima mwake mulibe kuopa Mulungu.
Керівнику хору. Псалом слуги Господнього, Давида. Промовляє беззаконня до нечестивця в глибинах його серця, немає страху Божого перед його очима.
2 Pakuti iye mʼkuona kwake amadzinyenga yekha kwambiri, sazindikira kapena kudana ndi tchimo lake.
Адже він так сам себе улещує в очах своїх, що не може знайти гріха в собі, щоб його зненавидіти.
3 Mawu a pakamwa pake ndi oyipa ndi achinyengo; iyeyo waleka kukhala wanzeru ndi kuchita zabwino.
Слова вуст його – беззаконня й підступ; він неспроможний мислити розсудливо й робити добро.
4 Ngakhale ali pa bedi pake amakonzekera zoyipa; iye amadzipereka yekha ku njira ya uchimo ndipo sakana cholakwa chilichonse.
Він задумує беззаконня [навіть] на своєму ложі, стає на недобрий шлях, не цурається зла.
5 Chikondi chanu Yehova, chimafika ku mayiko a kumwamba, kukhulupirika kwanu mpaka ku mitambo.
Господи, Твоя милість [сягає] небес, Твоя вірність – аж до хмар.
6 Chilungamo chanu Mulungu chili ngati mapiri aakulu, chiweruzo chanu chili ngati kuzama kwakukulu. Yehova mumasunga munthu pamodzi ndi chinyama.
Праведність Твоя – немов могутні гори, Твій [справедливий] суд – велика безодня. Людей і тварин Ти бережеш, Господи.
7 Chikondi chanu chosatha ndi chamtengowapatali! Otchuka pamodzi ndi anthu wamba pakati pa anthu amapeza pothawirapo mu mthunzi wa mapiko anu.
Яка дорогоцінна милість Твоя, Боже! Тому сини людські в тіні Твоїх крил спочивають безпечно.
8 Iwo amadyerera zinthu zambiri za mʼnyumba yanu; Inu mumawapatsa chakumwa kuchokera mu mtsinje wanu wachikondwerero.
Насичуються вони від достатку [благ] Твого дому, і потоком насолод Своїх Ти їх напуваєш.
9 Pakuti kwa Inu kuli kasupe wamoyo; mʼkuwala kwanu ifenso timaona kuwala.
Адже в Тебе джерело життя, у світлі Твоєму ми бачимо світло.
10 Pitirizani chikondi chanu pa iwo amene amakudziwani, chilungamo chanu kwa olungama mtima.
Продовж Свою милість для тих, хто Тебе знає, і праведність Свою – для щирих серцем.
11 Musalole kuti phazi la wodzikuza libwere kulimbana nane, kapena dzanja la oyipa kundithamangitsa.
Нехай не наступить на мене нога зухвалого, нехай не вижене мене рука нечестивого.
12 Onani momwe ochita zoyipa agonera atagwa, aponyeni pansi, kuti asathe kudzukanso!
[Поглянь-но: ] ось там упали ті, що чинять беззаконня, вони повалені й встати не можуть!