< Masalimo 36 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova. Uthenga uli mu mtima mwanga wonena za kuchimwa kwa munthu woyipa: Mu mtima mwake mulibe kuopa Mulungu.
Mivolañe an-karatiañe an-tro’e ao ty Tsivokatse. Toe tsy aolo’ o maso’eo ty fañeveñañe aman’ Añahare.
2 Pakuti iye mʼkuona kwake amadzinyenga yekha kwambiri, sazindikira kapena kudana ndi tchimo lake.
Mitsiriry ty vata’e o maso’eo, ie maharendreke te mavoeñe o sata’eo.
3 Mawu a pakamwa pake ndi oyipa ndi achinyengo; iyeyo waleka kukhala wanzeru ndi kuchita zabwino.
Tahiñe naho hakalitahañe o fivolam-bava’eo; nado’e ty hihitse tsy anoe’e ty hasoa.
4 Ngakhale ali pa bedi pake amakonzekera zoyipa; iye amadzipereka yekha ku njira ya uchimo ndipo sakana cholakwa chilichonse.
Mikitro-karatiañe an-tihi’e eo, mijohañ’ ami’ty lalañe tsy mahasoa; tsy rihie’e ty haloloañe.
5 Chikondi chanu Yehova, chimafika ku mayiko a kumwamba, kukhulupirika kwanu mpaka ku mitambo.
Ry Iehovà, mahatakatse an-dikerañe ao ty fiferenaiña’o, an-drahoñe eñe ty figahiña’o.
6 Chilungamo chanu Mulungu chili ngati mapiri aakulu, chiweruzo chanu chili ngati kuzama kwakukulu. Yehova mumasunga munthu pamodzi ndi chinyama.
Manahake o vohitse ra’elahio ty havantaña’o, miheotse o fizaka’oo, ry Iehovà, Hene ambena’o ndra ondaty ndra biby.
7 Chikondi chanu chosatha ndi chamtengowapatali! Otchuka pamodzi ndi anthu wamba pakati pa anthu amapeza pothawirapo mu mthunzi wa mapiko anu.
Fanjaka ty fiferenaiña’o, ry Andrianañahare! vaho mipalitse an-talinjon’ela’o ao o ana’ ondatio;
8 Iwo amadyerera zinthu zambiri za mʼnyumba yanu; Inu mumawapatsa chakumwa kuchokera mu mtsinje wanu wachikondwerero.
Ie anjañe ami’ty havokara’ o anjomba’oo, vaho ampikamae’o añ’oñen-karavoravoa’o.
9 Pakuti kwa Inu kuli kasupe wamoyo; mʼkuwala kwanu ifenso timaona kuwala.
Fa ama’o ty rano itsititiahan-kaveloñe; an-kazavà’o ao ro ahaoniña’ay hazavàñe.
10 Pitirizani chikondi chanu pa iwo amene amakudziwani, chilungamo chanu kwa olungama mtima.
Toloño amo mahafohiñ’Azoo ty fiferenaiña’o; naho amo vañon-trokeo ty havantaña’o.
11 Musalole kuti phazi la wodzikuza libwere kulimbana nane, kapena dzanja la oyipa kundithamangitsa.
Ee te tsy homb’amako ty tombom-pinevonevoke, vaho tsy hanao soik’ ahy ty tañan-do-tsereke.
12 Onani momwe ochita zoyipa agonera atagwa, aponyeni pansi, kuti asathe kudzukanso!
Mifitake ey o mpanao ratio, naronje ambane, tsy hitroatse ka.