< Masalimo 36 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova. Uthenga uli mu mtima mwanga wonena za kuchimwa kwa munthu woyipa: Mu mtima mwake mulibe kuopa Mulungu.
To the chief Musician, A Psalm of David the servant of the LORD. The transgression of the wicked saith within my heart, that there is no fear of God before his eyes.
2 Pakuti iye mʼkuona kwake amadzinyenga yekha kwambiri, sazindikira kapena kudana ndi tchimo lake.
For he flattereth himself in his own eyes, until his iniquity is found to be hateful.
3 Mawu a pakamwa pake ndi oyipa ndi achinyengo; iyeyo waleka kukhala wanzeru ndi kuchita zabwino.
The words of his mouth are iniquity and deceit: he hath ceased to be wise, and to do good.
4 Ngakhale ali pa bedi pake amakonzekera zoyipa; iye amadzipereka yekha ku njira ya uchimo ndipo sakana cholakwa chilichonse.
He deviseth mischief upon his bed; he setteth himself in a way that is not good; he abhorreth not evil.
5 Chikondi chanu Yehova, chimafika ku mayiko a kumwamba, kukhulupirika kwanu mpaka ku mitambo.
Thy mercy, O LORD, is in the heavens; and thy faithfulness reacheth to the clouds.
6 Chilungamo chanu Mulungu chili ngati mapiri aakulu, chiweruzo chanu chili ngati kuzama kwakukulu. Yehova mumasunga munthu pamodzi ndi chinyama.
Thy righteousness is like the great mountains; thy judgments are a great deep: O LORD, thou preservest man and beast.
7 Chikondi chanu chosatha ndi chamtengowapatali! Otchuka pamodzi ndi anthu wamba pakati pa anthu amapeza pothawirapo mu mthunzi wa mapiko anu.
How excellent is thy lovingkindness, O God! therefore the children of men put their trust under the shadow of thy wings.
8 Iwo amadyerera zinthu zambiri za mʼnyumba yanu; Inu mumawapatsa chakumwa kuchokera mu mtsinje wanu wachikondwerero.
They shall be abundantly satisfied with the fatness of thy house; and thou shalt make them drink of the river of thy pleasures.
9 Pakuti kwa Inu kuli kasupe wamoyo; mʼkuwala kwanu ifenso timaona kuwala.
For with thee is the fountain of life: in thy light shall we see light.
10 Pitirizani chikondi chanu pa iwo amene amakudziwani, chilungamo chanu kwa olungama mtima.
O continue thy lovingkindness to them that know thee; and thy righteousness to the upright in heart.
11 Musalole kuti phazi la wodzikuza libwere kulimbana nane, kapena dzanja la oyipa kundithamangitsa.
Let not the foot of pride come against me, and let not the hand of the wicked remove me.
12 Onani momwe ochita zoyipa agonera atagwa, aponyeni pansi, kuti asathe kudzukanso!
There are the workers of iniquity fallen: they are cast down, and shall not be able to rise.

< Masalimo 36 >