< Masalimo 36 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova. Uthenga uli mu mtima mwanga wonena za kuchimwa kwa munthu woyipa: Mu mtima mwake mulibe kuopa Mulungu.
[For the Chief Musician. By David, the servant of the LORD.] Transgression speaks to the wicked within his heart. There is no fear of God before his eyes.
2 Pakuti iye mʼkuona kwake amadzinyenga yekha kwambiri, sazindikira kapena kudana ndi tchimo lake.
For he flatters himself in his own eyes, too much to detect and hate his sin.
3 Mawu a pakamwa pake ndi oyipa ndi achinyengo; iyeyo waleka kukhala wanzeru ndi kuchita zabwino.
The words of his mouth are iniquity and deceit. He has ceased to be wise and to do good.
4 Ngakhale ali pa bedi pake amakonzekera zoyipa; iye amadzipereka yekha ku njira ya uchimo ndipo sakana cholakwa chilichonse.
He plots iniquity on his bed. He sets himself in a way that is not good. He doesn't abhor evil.
5 Chikondi chanu Yehova, chimafika ku mayiko a kumwamba, kukhulupirika kwanu mpaka ku mitambo.
Your loving kindness, LORD, is in the heavens. Your faithfulness reaches to the skies.
6 Chilungamo chanu Mulungu chili ngati mapiri aakulu, chiweruzo chanu chili ngati kuzama kwakukulu. Yehova mumasunga munthu pamodzi ndi chinyama.
Your righteousness is like the mountains of God. Your judgments are like a great deep. LORD, you preserve man and animal.
7 Chikondi chanu chosatha ndi chamtengowapatali! Otchuka pamodzi ndi anthu wamba pakati pa anthu amapeza pothawirapo mu mthunzi wa mapiko anu.
How precious is your loving kindness, God. The descendants of Adam take refuge under the shadow of your wings.
8 Iwo amadyerera zinthu zambiri za mʼnyumba yanu; Inu mumawapatsa chakumwa kuchokera mu mtsinje wanu wachikondwerero.
They shall be abundantly satisfied with the abundance of your house. You will make them drink of the river of your pleasures.
9 Pakuti kwa Inu kuli kasupe wamoyo; mʼkuwala kwanu ifenso timaona kuwala.
For with you is the spring of life. In your light shall we see light.
10 Pitirizani chikondi chanu pa iwo amene amakudziwani, chilungamo chanu kwa olungama mtima.
Oh continue your loving kindness to those who know you, your righteousness to the upright in heart.
11 Musalole kuti phazi la wodzikuza libwere kulimbana nane, kapena dzanja la oyipa kundithamangitsa.
Do not let the foot of pride come against me. Do not let the hand of the wicked drive me away.
12 Onani momwe ochita zoyipa agonera atagwa, aponyeni pansi, kuti asathe kudzukanso!
There evildoers are fallen. They are thrust down, and shall not be able to rise.

< Masalimo 36 >