< Masalimo 35 >
1 Salimo la Davide. Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane; mumenyane nawo amene akumenyana nane.
`To Dauid. Lord, deme thou hem, that anoien me; ouercome thou hem, that fiyten ayens me.
2 Tengani chishango ndi lihawo; dzukani ndipo bwerani mundithandize.
Take thou armeris and scheeld; and rise vp into help to me.
3 Tengani mkondo ndi nthungo, kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa. Uzani moyo wanga kuti, “Ine ndine chipulumutso chako.”
Schede out the swerd, and close togidere ayens hem that pursuen me; seie thou to my soule, Y am thin helthe.
4 Iwo amene akufunafuna moyo wanga anyozedwe ndi kuchita manyazi; iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.
Thei that seken my lijf; be schent, and aschamed. Thei that thenken yuels to me; be turned awei bacward, and be schent.
5 Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.
Be thei maad as dust bifor the face of the wynd; and the aungel of the Lord make hem streit.
6 Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.
Her weie be maad derknesse, and slydirnesse; and the aungel of the Lord pursue hem.
7 Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,
For with out cause thei hidden to me the deth of her snare; in veyn thei dispisiden my soule.
8 chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa ukonde umene iwo abisa uwakole, agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.
The snare which he knoweth not come to hym, and the takyng which he hidde take hym; and fall he in to the snare in that thing.
9 Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.
But my soule schal fulli haue ioye in the Lord; and schal delite on his helthe.
10 Thupi langa lidzafuwula mokondwera, “Ndani angafanane nanu Yehova? Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri, osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”
Alle my boonys schulen seie, Lord, who is lijk thee? Thou delyuerist a pore man fro the hond of his strengere; a nedi man and pore fro hem that diuersely rauischen hym.
11 Mboni zopanda chisoni zinayimirira, zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.
Wickid witnessis risynge axiden me thingis, whiche Y knewe not.
12 Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.
Thei yeldiden to me yuels for goodis; bareynnesse to my soule.
13 Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya. Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,
But whanne thei weren diseseful to me; Y was clothid in an heire. I mekide my soule in fastyng; and my preier schal be turned `with ynne my bosum.
14 ndinayendayenda ndi kulira maliro, kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga. Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima kukhala ngati ndikulira amayi anga.
I pleside so as oure neiybore, as oure brother; Y was `maad meke so as morenynge and sorewful.
15 Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala; ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa. Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.
And thei weren glad, and camen togidere ayens me; turmentis weren gaderid on me, and Y knew not.
16 Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe; anandikukutira mano awo.
Thei weren scaterid, and not compunct, thei temptiden me, thei scornyden me with mowyng; thei gnastiden on me with her teeth.
17 Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana? Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo, moyo wanga wopambana ku mikango.
Lord, whanne thou schalt biholde, restore thou my soule fro the wickidnesse of hem; `restore thou myn oon aloone fro liouns.
18 Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu; pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.
I schal knowleche to thee in a greet chirche; Y schal herie thee in a sad puple.
19 Musalole adani anga onyenga akondwere chifukwa cha masautso anga; musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.
Thei that ben aduersaries wickidli to me, haue not ioye on me; that haten me with out cause, and bikenen with iyen.
20 Iwowo sayankhula mwamtendere, koma amaganizira zonamizira iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.
For sotheli thei spaken pesibli to me; and thei spekynge in wrathfulnesse of erthe thouyten giles.
21 Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa! Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”
And thei maden large her mouth on me; thei seiden, Wel, wel! oure iyen han sien.
22 Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete. Ambuye musakhale kutali ndi ine.
Lord, thou hast seen, be thou not stille; Lord, departe thou not fro me.
23 Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza! Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.
Rise vp, and yyue tent to my doom; my God and my Lord, biholde in to my cause.
24 Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga. Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.
Mi Lord God, deme thou me bi thi riytfulnesse; and haue thei not ioye on me.
25 Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!” Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”
Seie thei not in her hertis, Wel, wel, to oure soule; nether seie thei, We schulen deuoure hym.
26 Onse amene amakondwera ndi masautso anga achite manyazi ndi kusokonezeka. Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana, avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.
Shame thei, and drede thei togidere; that thanken for myn yuels. Be thei clothid with schame and drede; that speken yuele thingis on me.
27 Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa, afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo. Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke, Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”
Haue thei ful ioie, and be thei glad that wolen my riytfulnesse; and seie thei euere, The Lord be magnyfied, whiche wolen the pees of his seruaunt.
28 Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu ndi za matamando anu tsiku lonse.
And my tunge schal bithenke thi riytfulnesse; al day thin heriyng.