< Masalimo 35 >
1 Salimo la Davide. Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane; mumenyane nawo amene akumenyana nane.
“Of David.” Contend, O Lord, with those that contend with me: fight against those that fight against me.
2 Tengani chishango ndi lihawo; dzukani ndipo bwerani mundithandize.
Take hold of shield and buckler, and rise up for my help.
3 Tengani mkondo ndi nthungo, kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa. Uzani moyo wanga kuti, “Ine ndine chipulumutso chako.”
And draw out the spear, and step in against my pursuers; say unto my soul, I am thy salvation.
4 Iwo amene akufunafuna moyo wanga anyozedwe ndi kuchita manyazi; iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.
Let those be put to shame and be confounded that seek after my life: let those be turned backward and be made to blush, that devise unhappiness for me.
5 Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.
Let them be as chaff before the wind; and may the angel of the Lord cast them forth.
6 Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.
May their way be dark and slippery: and may the angel of the Lord pursue them.
7 Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,
For without cause have they hidden for me their net in a pit, without cause have they dug [pit-falls] against my life.
8 chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa ukonde umene iwo abisa uwakole, agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.
May then destruction come upon each of them at unawares; and may his net that he hath hidden catch himself: in [utter] destruction let him fall therein.
9 Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.
But my soul shall exult in the Lord: she shall be glad through his salvation.
10 Thupi langa lidzafuwula mokondwera, “Ndani angafanane nanu Yehova? Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri, osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”
All my bones will say, Lord, who is like unto thee, who deliverest the poor from him that is too strong for him, yea, the poor and the needy from him that robbeth him?
11 Mboni zopanda chisoni zinayimirira, zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.
There rise up witnesses of violence; concerning what I know not they question me.
12 Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.
They recompense me with evil in place of good, [bringing] bereavement on my soul.
13 Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya. Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,
But as for me, when they were sick, my clothing was sackcloth: I afflicted with fasting my soul, and my prayer returned into my own bosom.
14 ndinayendayenda ndi kulira maliro, kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga. Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima kukhala ngati ndikulira amayi anga.
As though he had been to me a friend or a brother did I walk about: as one that mourneth for a mother did I sorrowfully bend down my head.
15 Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala; ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa. Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.
But in my downfall they rejoiced, and gathered themselves together; there gathered themselves together against me abject wretches, whom I knew not; they did tear me, and ceased not:
16 Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe; anandikukutira mano awo.
With hypocritical babbling mockers, they gnashed upon me with their teeth.
17 Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana? Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo, moyo wanga wopambana ku mikango.
O Lord, how long wilt thou look on? rescue my soul from their destructions, from the young lions my solitary spirit.
18 Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu; pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.
I will thank thee in the great assembly: among a mighty people will I praise thee.
19 Musalole adani anga onyenga akondwere chifukwa cha masautso anga; musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.
Let not rejoice over me those that are my enemies wrongfully: [nor] let those who hate me without cause wink with the eye.
20 Iwowo sayankhula mwamtendere, koma amaganizira zonamizira iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.
For they speak not peace; but against the quiet in the land they devise deceitful words.
21 Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa! Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”
Yea, they opened wide against me their mouth; they said, Aha, aha, our eye hath seen it.
22 Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete. Ambuye musakhale kutali ndi ine.
Thou hast seen it, O Lord! remain not silent: O Lord, be not far from me.
23 Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza! Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.
Arouse thyself, and awake to do me justice, my God and my Lord, unto my cause.
24 Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga. Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.
Judge me according to thy righteousness, O Lord my God; and let them not rejoice over me.
25 Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!” Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”
Let them not say in their heart, Aha, [this is the wish of] our soul: let them not say, We have swallowed him up.
26 Onse amene amakondwera ndi masautso anga achite manyazi ndi kusokonezeka. Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana, avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.
Let those be made ashamed and put to the blush together that rejoice at my mishap; let them be clothed with shame and confusion that magnify themselves above me.
27 Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa, afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo. Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke, Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”
Let those shout, and rejoice, that desire my righteousness: yea, let them say continually, Great is the Lord, who desireth the welfare of his servant.
28 Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu ndi za matamando anu tsiku lonse.
And my tongue shall speak of thy righteousness, all the day of thy praise.