< Masalimo 35 >

1 Salimo la Davide. Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane; mumenyane nawo amene akumenyana nane.
Žalm Davidův. Suď se, Hospodine, s těmi, kteříž se se mnou soudí; bojuj proti těm, kteříž proti mně bojují.
2 Tengani chishango ndi lihawo; dzukani ndipo bwerani mundithandize.
Pochyť štít a pavézu, a povstaň mi ku pomoci.
3 Tengani mkondo ndi nthungo, kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa. Uzani moyo wanga kuti, “Ine ndine chipulumutso chako.”
Vezmi i kopí, a vyjdi vstříc těm, kteříž táhnou proti mně. Rciž duši mé: Spasení tvé jáť jsem.
4 Iwo amene akufunafuna moyo wanga anyozedwe ndi kuchita manyazi; iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.
Nechať se zahanbí a zapýří ti, kteříž hledají duše mé; zpět ať jsou obráceni a zahanbeni ti, kteříž mi zlé obmýšlejí.
5 Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.
Ať jsou jako plevy před větrem, a anděl Hospodinův rozptylujž je.
6 Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.
Cesta jejich budiž temná a plzká, a anděl Hospodinův stihej je.
7 Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,
Nebo jsou bez příčiny polékli v jámě osídlo své, bez příčiny vykopali jámu duši mé.
8 chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa ukonde umene iwo abisa uwakole, agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.
Připadniž na ně setření, jehož se nenadáli, a sít jejich, kterouž ukryli, ať je uloví; s hřmotem ať do ní vpadnou.
9 Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.
Duše má pak ať se veselí v Hospodinu, a ať raduje se v spasení jeho.
10 Thupi langa lidzafuwula mokondwera, “Ndani angafanane nanu Yehova? Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri, osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”
A tuť všecky kosti mé řeknou: Hospodine, kdo jest podobný tobě, ješto vytrhuješ ztrápeného z moci toho, kterýž nad něj silnější jest, tolikéž chudého a nuzného od toho, kterýž ho násilně loupí?
11 Mboni zopanda chisoni zinayimirira, zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.
Povstávají svědkové lživí, a na to, o čemž nevím, dotazují se mne.
12 Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.
Zlým za dobré mi se odplacují, duše mé zbaviti mne chtíce,
13 Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya. Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,
Ježto já v nemoci jejich pytlem jsem se přiodíval, duši svou postem trápil, a sám u sebe za ně často se modlil.
14 ndinayendayenda ndi kulira maliro, kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga. Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima kukhala ngati ndikulira amayi anga.
Jako k příteli, jako k bratru vlastnímu jsem chodíval; jakožto ten, kterýž po matce kvílí, smutek nesa, tak jsem se ponižoval.
15 Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala; ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa. Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.
Ale oni z mého zlého radovali se, a rotili se; shromažďovali se proti mně i ti nejnevážnější, o čemž jsem nevěděl; utrhali mi, a nemlčeli.
16 Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe; anandikukutira mano awo.
S pokrytci, posměvači, fatkáři škřipěli na mne zuby svými.
17 Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana? Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo, moyo wanga wopambana ku mikango.
Pane, dlouho-liž se dívati budeš? Vytrhni duši mou od zhouby jejich, od lvů jedinkou mou.
18 Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu; pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.
I budu tě oslavovati v shromáždění velikém, ve množství lidu tebe chváliti budu.
19 Musalole adani anga onyenga akondwere chifukwa cha masautso anga; musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.
Nechažť se nade mnou neradují ti, kteříž bezprávně ke mně se nepřátelsky mají; ti, kteříž mne nenávidí bez příčiny, ať nemhourají očima.
20 Iwowo sayankhula mwamtendere, koma amaganizira zonamizira iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.
Neboť nemluví ku pokoji, ale proti pokojným na zemi slova lstivá vymýšlejí.
21 Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa! Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”
Anobrž rozdírají proti mně ústa svá, a říkají: Hahá, hahá, jižť vidí oko naše.
22 Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete. Ambuye musakhale kutali ndi ine.
Vidíš ty to, Hospodine, neodmlčujž se, Pane, nevzdalujž se ode mne.
23 Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza! Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.
Probudiž se a prociť k soudu mému, Bože můj a Pane můj, k obhájení pře mé.
24 Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga. Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.
Suď mne podlé spravedlnosti své, Hospodine Bože můj, ať se neradují nade mnou.
25 Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!” Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”
Ať neříkají v srdci svém: Měhoděk duši naší; ať neříkají: Sehltili jsme jej.
26 Onse amene amakondwera ndi masautso anga achite manyazi ndi kusokonezeka. Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana, avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.
Ale ať se zahanbí a zapýří všickni radující se mému zlému, v stud a hanbu ať jsou oblečeni ti, kteříž se zpínají proti mně.
27 Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa, afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo. Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke, Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”
Ti pak, kteříž mi přejí mé spravedlnosti, ať plésají, a radují se, a ať říkají vždycky: Veleslaven budiž Hospodin, kterýž přeje pokoje služebníku svému.
28 Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu ndi za matamando anu tsiku lonse.
I můj jazyk ohlašovati bude spravedlnost tvou, a na každý den chválu tvou.

< Masalimo 35 >