< Masalimo 34 >
1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
Давидів, коли він удавав був причи́нного перед Авімелехом, що вигнав його, і той пішов. Я благословля́тиму Господа кожного ча́су, хвала́ Йому за́всіди в у́стах моїх!
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
Душа моя буде хвалитися Господом, — хай це почують слухня́ні, і нехай звеселяться!
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
Зо мною звели́чуйте Господа, і підносьте Ім'я́ Його ра́зом!
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
Шукав я був Господа, — і Він озвався до мене, і від усіх небезпе́к мене ви́зволив.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
Приглядайтесь до Нього — й зася́єте, і не посоро́мляться ваші обличчя!
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
Цей убогий взивав, — і Господь його ви́слухав, і від усіх його бід його ви́зволив.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
Ангол Господній табо́ром стає кругом тих, хто боїться його́, — і визво́лює їх.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Скушту́йте й побачте, який добрий Госпо́дь, блаженна люди́на, що надію на Нього кладе́!
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
Бійтеся Господа, всі святії Його, бо ті, що бояться Його, недостатку не мають!
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
Левчуки́ бідні й голодні, а ті, хто пошукує Господа, недостатку не чують в усьому добрі́.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Ходіть, діти, послухайте мене, — стра́ху Господнього я вас навчу!
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
Хто та людина, що хоче життя, що любить дні довгі, щоб бачити добро́?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Свого язика́ бережи від лихого, а уста свої — від гово́рений пі́дступу.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Відступися від злого і добре чини, миру шукай і женися за ним!
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
Очі Господні на праведних, уші ж Його — на їхній зойк,
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
Господнє лице — на злочинців, щоб ви́нищити їхню пам'ять з землі.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
Коли пра́ведні кли́чуть, то їх чує Господь, і з усіх утисків їхніх визво́лює їх.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
Господь зламаносе́рдим близьки́й, і впоко́рених духом спасає.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Багато лихого для праведного, та його визволя́є Господь з них усіх:
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
Він пильнує всі кості його, — із них жо́дна не зламається!
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
Зло безбожному смерть заподіє, і винними будуть усі, хто нена́видить праведного.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
Господь ви́зволить душу рабів Своїх, і винні не будуть усі, хто вдається до Нього!