< Masalimo 34 >
1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
Davut'un mezmuru Avimelek'in önünde kendini deli gösterip kovulduğu, gittiği zaman Her zaman RAB'be övgüler sunacağım, Övgüsü dilimden düşmeyecek.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
RAB'le övünürüm, Mazlumlar işitip sevinsin!
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
Benimle birlikte RAB'bin büyüklüğünü duyurun, Adını birlikte yüceltelim.
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
RAB'be yöneldim, yanıt verdi bana, Bütün korkularımdan kurtardı beni.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
O'na bakanların yüzü ışıl ışıl parlar, Yüzleri utançtan kızarmaz.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
Bu mazlum yakardı, RAB duydu, Bütün sıkıntılarından kurtardı onu.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
RAB'bin meleği O'ndan korkanların çevresine ordugah kurar, Kurtarır onları.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Tadın da görün, RAB ne iyidir, Ne mutlu O'na sığınan adama!
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
RAB'den korkun, ey O'nun kutsalları, Çünkü O'ndan korkanın eksiği olmaz.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
Genç aslanlar bile aç ve muhtaç olur; Ama RAB'be yönelenlerden hiçbir iyilik esirgenmez.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Gelin, ey çocuklar, dinleyin beni: Size RAB korkusunu öğreteyim.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
Kim yaşamdan zevk almak, İyi günler görmek istiyorsa,
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Dilini kötülükten, Dudaklarını yalandan uzak tutsun.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Kötülükten sakının, iyilik yapın; Esenliği amaçlayın, ardınca gidin.
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
RAB'bin gözleri doğru kişilerin üzerindedir, Kulakları onların yakarışına açıktır.
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
RAB kötülük yapanlara karşıdır, Onların anısını yeryüzünden siler.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
Doğrular yakarır, RAB duyar; Bütün sıkıntılarından kurtarır onları.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
RAB gönlü kırıklara yakındır, Ruhu ezikleri kurtarır.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Doğrunun dertleri çoktur, Ama RAB hepsinden kurtarır onu.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
Bütün kemiklerini korur, Hiçbiri kırılmaz.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
Kötü insanın sonu kötülükle biter, Cezasını bulur doğrulardan nefret edenler.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
RAB kullarını kurtarır, O'na sığınanların hiçbiri ceza görmez.