< Masalimo 34 >

1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
Un salmo de David sobre la vez que aparentó estar loco frente a Abimelec, quien lo echó de su presencia. Siempre alabaré al Señor; mi boca continuamente lo alabará.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
Estoy orgulloso del Señor desde lo profundo de mi corazón; aquellos que son humildes oirán y serán felices.
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
Glorifiquen al Señor conmigo; honremos juntos su nombre.
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
Clamé al Señor por ayuda, y él me respondió. Me liberó de todos mis miedos.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
Las caras de aquellos que lo miran brillaran de alegría. Nunca serán abatidos con vergüenza.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
Este pobre hombre lloró, y el Señor me oyó, y me salvó de todos mis problemas.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
El ángel del Señor permanece vigilante sobre los que le honran, manteniéndolos a salvo.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
¡Prueba, y verás que el Señor es bueno! ¡Cuán felices son los que creen su protección!
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
Muestra tu reverencia al Señor, tú que eres su pueblo santo, porque a los que lo respetan no les faltará nada.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
Los leones pueden crecer débiles y hambrientos, pero los que confían en el Señor tienen todo lo que es bueno.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
¡Niños, escúchenme! Les enseñaré como respetar al Señor.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
¿Quién de ustedes quiere vivir una vida larga y feliz?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Entonces no dejen que sus lenguas hablen maldad, o que sus labios digan mentiras.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Rechacen lo malo, hagan lo bueno. Busquen la paz, y trabajen para hacerla realidad.
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
El Señor cuida a los que hacen lo correcto, y escucha cuando claman por ayuda.
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
El Señor es enemigo de los que hacen el mal. Él borrará hasta la memoria de ellos de la tierra.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
Pero cuando su pueblo llama pidiendo ayuda, él los escucha y los rescata de sus problemas.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
El Señor está cerca de los que tienen el corazón roto. Él salva a aquellos cuyo espíritu está quebrantado.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Aquellos que hacen lo correcto tienen muchos problemas, pero el Señor los resuelve todos.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
Él los mantiene a salvo, ni uno de sus huesos se romperá.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
La maldad mata a los malvados. Aquellos que odian a la gente buena sufrirán por sus malos actos.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
El Señor protege la vida de sus siervos. Aquellos que confían en su protección no sufrirán por sus acciones equivocadas.

< Masalimo 34 >