< Masalimo 34 >

1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
Blagosiljam Gospoda u svako doba, hvala je njegova svagda u ustima mojima.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
Gospodom se hvali duša moja; neka èuju koji stradaju, pa neka se raduju.
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
Velièajte Gospoda sa mnom, uzvišujmo ime njegovo zajedno.
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
Tražih Gospoda, i èu me, i svijeh nevolja mojih oprosti me.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
Koji u njega gledaju prosvjetljuju se, i lica se njihova neæe postidjeti.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
Ovaj stradalac zavika, i Gospod ga èu, i oprosti ga svijeh nevolja njegovijeh.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
Anðeli Gospodnji stanom stoje oko onijeh koji se njega boje, i izbavljaju ih.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Ispitajte i vidite kako je dobar Gospod; blago èovjeku koji se uzda u nj.
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
Bojte se Gospoda, sveti njegovi; jer koji se njega boje, njima nema oskudice.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
Lavovi su ubogi i gladni, a koji traže Gospoda, ne premièe im se nijednoga dobra.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Hodite, djeco, poslušajte me; nauèiæu vas strahu Gospodnjemu.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
Koji èovjek želi života, ljubi dane da bi vidio dobro?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Ustavljaj jezik svoj oda zla, i usta svoja od prijevarne rijeèi.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Kloni se oda zla, i èini dobro, traži mira i idi za njim.
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
Oèi su Gospodnje obraæene na pravednike, i uši njegove na jauk njihov.
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
Ali je strašno lice Gospodnje za one koji èine zlo, da bi istrijebio na zemlji spomen njihov.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
Vièu pravedni, i Gospod ih èuje, i izbavlja ih od svijeh nevolja njihovijeh.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
Gospod je blizu onijeh koji su skrušena srca, i pomaže onima koji su smjerna duha.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Mnogo nevolje ima pravednik, ali ga od svijeh izbavlja Gospod.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
Èuva Gospod sve kosti njegove, nijedna se od njih neæe slomiti.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
Bezbožnika ubiæe zlo, i koji nenavide pravednika prevariæe se.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
Gospod iskupljuje dušu sluga svojih, i koji se god u njega uzdaju, neæe se prevariti.

< Masalimo 34 >