< Masalimo 34 >

1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
ElikaDavida. Lapho azenza uhlanya ku-Abhimelekhi, owamxotshayo wahamba. Ngizamphakamisa uThixo ngezikhathi zonke; indumiso yakhe izahlala isezindebeni zami.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
Umphefumulo wami uzaziqhenya Thixo akuthi abahluphekileyo bezwe bajabule.
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
Bongani uThixo kanye lami; kasiphakamiseni ibizo lakhe sonke, ndawonye.
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
Ngamdinga uThixo wangiphendula; wangikhulula kukho konke engangikwesaba.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
Labo abakhangele Kuye bayakhazimula; ubuso babo abungeke bembeswe lihlazo.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
Isihlupheki lesi samemeza, uThixo wasizwa; wasisindisa kuzozonke inhlupheko zaso.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
Ingilosi kaThixo iyabazungeza labo abamesabayo, ibakhulule.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Nambithani libone ukuthi uThixo ulungile; ubusisiwe umuntu ophephela Kuye.
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
Mesabeni Uthixo, lina bangcwele bakhe, ngoba labo abamesabayo kabasweli lutho.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
Izilwane zingaphela amandla zilambe, kodwa labo abamdingayo uThixo kabasweli lutho oluhle.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Wozani, bantwabami, lalelani kimi; ngizalifundisa ukumesaba uThixo.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
Lowo othanda ukuphila abone lezinsuku ezinhle kumele
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
anqande ulimi lwakhe kokubi lezindebe zakhe ekukhulumeni inkohliso.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Tshiya ububi wenze okulungileyo; funa ukuthula ukunxwanele.
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
Amehlo kaThixo akhangele abalungileyo lezindlebe zakhe ziyezwa ukukhala kwabo;
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
ubuso bukaThixo bumelana lalabo abenza okubi, ukuba acitshe ukukhunjulwa kwabo emhlabeni.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
Abalungileyo bayakhala kuThixo abezwe; uyabakhulula kuzozonke inhlupheko zabo.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
UThixo useduze labo abalezinhliziyo ezephukileyo asindise labo abadabukileyo emoyeni.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Umuntu olungileyo angaba lezinhlupheko ezinengi, kodwa uThixo uyamkhulula kuzozonke.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
Uyawavikela wonke amathambo akhe, kungephuki loba lalinye.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
Ububi buzambulala oyisixhwali; izitha zolungileyo zizalahlwa.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
UThixo uyazihlenga izinceku zakhe; kakho ozalahlwa ophephela kuye.

< Masalimo 34 >