< Masalimo 34 >

1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
Di Davide, quando si finse pazzo in presenza di Abimelech e, da lui scacciato, se ne andò. Benedirò il Signore in ogni tempo, sulla mia bocca sempre la sua lode.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
Io mi glorio nel Signore, ascoltino gli umili e si rallegrino.
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
Celebrate con me il Signore, esaltiamo insieme il suo nome.
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
Ho cercato il Signore e mi ha risposto e da ogni timore mi ha liberato.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
Guardate a lui e sarete raggianti, non saranno confusi i vostri volti.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
Questo povero grida e il Signore lo ascolta, lo libera da tutte le sue angosce.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
L'angelo del Signore si accampa attorno a quelli che lo temono e li salva.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Gustate e vedete quanto è buono il Signore; beato l'uomo che in lui si rifugia.
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
Temete il Signore, suoi santi, nulla manca a coloro che lo temono.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
I ricchi impoveriscono e hanno fame, ma chi cerca il Signore non manca di nulla.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Venite, figli, ascoltatemi; v'insegnerò il timore del Signore.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
C'è qualcuno che desidera la vita e brama lunghi giorni per gustare il bene?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Preserva la lingua dal male, le labbra da parole bugiarde.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Stà lontano dal male e fà il bene, cerca la pace e perseguila.
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
Gli occhi del Signore sui giusti, i suoi orecchi al loro grido di aiuto.
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
Il volto del Signore contro i malfattori, per cancellarne dalla terra il ricordo.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
Gridano e il Signore li ascolta, li salva da tutte le loro angosce.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
Il Signore è vicino a chi ha il cuore ferito, egli salva gli spiriti affranti.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Molte sono le sventure del giusto, ma lo libera da tutte il Signore.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
Preserva tutte le sue ossa, neppure uno sarà spezzato.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
La malizia uccide l'empio e chi odia il giusto sarà punito.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
Il Signore riscatta la vita dei suoi servi, chi in lui si rifugia non sarà condannato.

< Masalimo 34 >