< Masalimo 34 >
1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
Von David, da er seine Gebärde verstellte vor Abimelech, und dieser ihn forttrieb, und er ging. Ich will Jehovah segnen alle Zeit; Sein Lob soll beständig in meinem Munde sein.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
Jehovahs rühme meine Seele sich; die Elenden sollen es hören und fröhlich sein.
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
Machet groß mit mir Jehovah, laßt uns erhöhen Seinen Namen allzumal.
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
Ich fragte nach Jehovah, und Er antwortete mir und errettete mich aus all meinem Bangen.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
Sie blicken zu Ihm auf und strahlen. Und ihr Angesicht darf nicht erröten.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
Es rief dieser Elende, und Jehovah hörte ihn, und rettete ihn aus allen seinen Drangsalen.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
Jehovahs Engel lagert sich rings um die, so Ihn fürchten, und Er zieht sie heraus.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Schmecket und sehet, wie gut Jehovah ist. Selig der Mann, der auf Ihn sich verläßt.
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
Fürchtet Jehovah, ihr Seine Heiligen; denn denen, die Ihn fürchten, mangelt nichts.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
Die jungen Löwen darben und hungern; aber denen, die nach Jehovah fragen, mangelt es an keinem Gut.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Kommt, Söhne, höret mir zu, ich will euch die Furcht Jehovahs lehren.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
Wer ist der Mann, der Lust hat am Leben, und die Tage liebt, Gutes zu sehen?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Bewahre deine Zunge vor Bösem und deine Lippen, daß sie nicht Trug reden.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Weiche ab vom Bösen und tue Gutes. Suche Frieden und setze ihm nach.
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
Die Augen Jehovahs sind auf den Gerechten und Seine Ohren auf ihrem Angstschrei.
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
Das Angesicht Jehovahs ist wider die, so Böses tun, daß Er ihr Gedächtnis ausrotte von der Erde.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
Schreien jene, so hört Jehovah und errettet sie aus allen ihren Drangsalen.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
Jehovah ist denen nahe, die gebrochenen Herzens sind, und hilft denen, die einen zerschlagenen Geist haben.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Viel sind der Übel des Gerechten, aus allen aber errettet ihn Jehovah.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
Alle seine Gebeine hütet Er, daß keines ihm zerbrochen wird.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
Den Ungerechten tötet das Böse, und die den Gerechten hassen, werden schuldig.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
Jehovah löset die Seele Seiner Knechte ein, und alle, die auf Ihn sich verlassen, haben keine Schuld.