< Masalimo 34 >

1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
Je bénirai l'Éternel en tout temps; sa louange sera continuellement dans ma bouche.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
Mon âme se glorifiera en l'Éternel; les débonnaires l'entendront et se réjouiront.
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
Magnifiez l'Éternel avec moi; exaltons son nom tous ensemble!
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
J'ai cherché l'Éternel, et il m'a répondu; il m'a délivré de toutes mes frayeurs.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
L'a-t-on regardé? on en est illuminé, on n'a pas à rougir de honte.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
Cet affligé a crié, et l'Éternel l'a exaucé, et l'a délivré de toutes ses détresses.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
L'ange de l'Éternel campe autour de ceux qui le craignent, et il les délivre.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Goûtez et voyez combien l'Éternel est bon! Heureux l'homme qui se retire vers lui!
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
Craignez l'Éternel, vous ses saints, car rien ne manque à ceux qui le craignent!
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
Les lionceaux ont disette et ont faim; mais ceux qui cherchent l'Éternel n'auront faute d'aucun bien.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Venez, enfants, écoutez-moi; je vous enseignerai la crainte de l'Éternel.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
Quel est l'homme qui prenne plaisir à vivre, qui aime à voir des jours de bonheur?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Garde ta langue du mal, et tes lèvres de proférer la tromperie.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Détourne-toi du mal, et fais le bien; cherche la paix, et la poursuis.
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
Les yeux de l'Éternel sont sur les justes, et ses oreilles sont attentives à leur cri.
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
La face de l'Éternel est contre ceux qui font le mal, pour retrancher de la terre leur mémoire.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
Quand les justes crient, l'Éternel les exauce, et il les délivre de toutes leurs détresses.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
L'Éternel est près de ceux qui ont le cœur brisé, et il délivre ceux qui ont l'esprit froissé.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Le juste a des maux en grand nombre; mais l'Éternel le délivre de tous.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
Il garde tous ses os; aucun d'eux n'est rompu.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
Le mal fera mourir le méchant, et ceux qui haïssent le juste seront détruits.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
L'Éternel rachète l'âme de ses serviteurs, et aucun de ceux qui se retirent vers lui ne sera détruit.

< Masalimo 34 >