< Masalimo 34 >

1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
“A psalm of David, when he feigned himself mad before Abimelech, who drove him away, and he departed.” I will bless the LORD at all times; His praise shall continually be in my mouth.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
In the LORD doth my soul boast; Let the afflicted hear, and rejoice!
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
O magnify the LORD with me, And let us exalt his name together!
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
I sought the LORD, and he heard me, And delivered me from all my fears.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
Look up to him, and ye shall have light; Your faces shall never be ashamed.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
This afflicted man cried, and the LORD heard, And saved him from all his troubles.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
The angels of the LORD encamp around those who fear him, And deliver them.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
O taste, and see how good is the LORD! Happy the man who trusteth in him!
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
O fear the LORD, ye his servants! For to those who fear him there shall be no want.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
Young lions want, and suffer hunger; But they who fear the LORD want no good thing.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Come, ye children, hearken to me! I will teach you the fear of the LORD.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
Who is he that loveth life, And desireth many days, in which he may see good?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Guard well thy tongue from evil, And thy lips from speaking guile!
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Depart from evil, and do good; Seek peace, and pursue it!
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
The eyes of the LORD are upon the righteous, And his ears are open to their cry.
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
But the face of the LORD is against evil-doers, To cut off their remembrance from the earth.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
The righteous cry, and the LORD heareth, And delivereth them from all their troubles.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
The LORD is near to them that are of a broken heart, And saveth such as are of a contrite spirit.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Many are the afflictions of the righteous; But the LORD delivereth him from them all.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
He guardeth all his bones; Not one of them shall be broken.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
Calamity destroyeth the wicked, And they who hate the righteous suffer for it.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
The LORD redeemeth the life of his servants, And none that put their trust in him will suffer for it.

< Masalimo 34 >