< Masalimo 34 >

1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
[A Psalm] of David; when he changed his behaviour before Abimelech, who drove him away, and he departed. I will bless Jehovah at all times; his praise shall continually be in my mouth.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
My soul shall make its boast in Jehovah: the meek shall hear, and rejoice.
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
Magnify Jehovah with me, and let us exalt his name together.
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
I sought Jehovah, and he answered me, and delivered me from all my fears.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
They looked unto him, and were enlightened, and their faces were not confounded.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
This afflicted one called, and Jehovah heard [him], and saved him out of all his troubles.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
The angel of Jehovah encampeth round about them that fear him, and delivereth them.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Taste and see that Jehovah is good: blessed is the man that trusteth in him!
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
Fear Jehovah, ye his saints; for there is no want to them that fear him.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
The young lions are in need and suffer hunger; but they that seek Jehovah shall not want any good.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Come, ye sons, hearken unto me: I will teach you the fear of Jehovah.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
What man is he that desireth life, [and] loveth days, that he may see good?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Keep thy tongue from evil, and thy lips from speaking guile;
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Depart from evil, and do good; seek peace, and pursue it.
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
The eyes of Jehovah are upon the righteous, and his ears are toward their cry;
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
The face of Jehovah is against them that do evil, to cut off the remembrance of them from the earth:
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
[The righteous] cry, and Jehovah heareth, and delivereth them out of all their troubles.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
Jehovah is nigh to those that are of a broken heart, and saveth them that are of a contrite spirit.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Many are the adversities of the righteous, but Jehovah delivereth him out of them all:
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
He keepeth all his bones; not one of them is broken.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
Evil shall destroy the wicked; and they that hate the righteous shall bear their guilt.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
Jehovah redeemeth the soul of his servants; and none of them that trust in him shall bear guilt.

< Masalimo 34 >