< Masalimo 34 >

1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
Davidov. Kada se David pravio ludim pred Abimelekom, a on ALEF Blagoslivljat ću Jahvu u svako doba, njegova će mi hvala biti svagda na ustima!
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
BET Nek' se Jahvom duša moja hvali: nek' čuju ponizni i nek' se raduju!
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
GIMEL Veličajte sa mnom Jahvu, uzvisujmo ime njegovo zajedno!
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
DALETTražio sam Jahvu, i on me usliša, izbavi me od straha svakoga.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
HE U njega gledajte i razveselite se, da se ne postide lica vaša.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
ZAJIN Eto, jadnik vapi, a Jahve ga čuje, izbavlja ga iz svih tjeskoba.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
HET Anđeo Jahvin tabor podiže oko njegovih štovalaca da ih spasi.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
TET Kušajte i vidite kako dobar je Jahve: blago čovjeku koji se njemu utječe!
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
JOD Bojte se Jahve, vi sveti njegovi: ne trpe oskudice koji ga se boje.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
KAF Osiromašiše mogućnici i gladuju, a koji traže Jahvu ne trpe oskudice.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
LAMED Dođite, djeco, i poslušajte me, učit ću vas strahu Gospodnjem.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
MEM O čovječe, ljubiš li život? Želiš li dane mnoge uživati dobra?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
NUN Jezik svoj oda zla suspreži i usne od riječi prijevarnih!
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
SAMEK Zla se kloni, a čini dobro, traži mir i za njim idi!
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
PE Oči Jahvine gledaju pravedne, uši mu slušaju vapaje njihove.
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
AJIN Lice se Jahvino okreće protiv zločinaca da im spomen zatre na zemlji.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
SADE Pravednici zazivaju, i Jahve ih čuje, izbavlja ih iz svih tjeskoba.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
KOF Blizu je Jahve onima koji su skršena srca, a klonule duše spasava.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
REŠ Mnoge nevolje ima pravednik, ali ga Jahve od svih izbavlja.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
ŠIN On čuva sve kosti njegove: ni jedna mu se neće slomiti.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
TAU Opakost bezbošca ubija, platit će koji mrze pravednika.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
Jahve izbavlja duše slugu svojih, i neće platiti tko god se njemu utječe.

< Masalimo 34 >