< Masalimo 33 >

1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Fröjder eder af Herranom, I rättfärdige; de fromme skola prise honom härliga.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Tacker Herranom med harpor; och lofsjunger honom på psaltare af tio stränger.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Sjunger honom en ny viso; sjunger väl på strängaspel med klingande ljud.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
Ty Herrans ord är sannfärdigt; och hvad han lofvar, det håller han visserliga.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
Han älskar rättfärdighet och dom; jorden är full af Herrans godhet.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
Himmelen är gjord genom Herrans ord, och all hans här genom hans muns anda.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Han håller vattnet i hafvet tillsammans, såsom uti en lägel; och lägger djupen i det fördolda.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
All verlden frukte Herran; honom rädes allt det som på jordene bor.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
Ty om han säger, så sker det; om han bjuder, så är det gjordt.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
Herren gör Hedningarnas råd omintet, och vänder folks tankar.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
Men Herrans råd blifver evinnerliga; hans hjertas tankar i evighet.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Saligt är det folk, hvilkets Gud Herren är; det folk, som han till ett arf utkorat hafver.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
Herren skådar neder af himmelen, och ser all menniskors barn.
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
Utaf sinom fasta stol ser han uppå alla de som på jordene bo.
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
Han böjer allas deras hjerta; han aktar uppå alla deras gerningar.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
Enom Konung hjelper intet hans stora magt; enom kämpa varder icke hulpet genom hans stora kraft.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
Hästar hjelpa ock intet, och deras stora starkhet frälsar intet.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Si, Herrans öga ser uppå dem som frukta honom; de som uppå hans godhet trösta;
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
Att han skall fria deras själ ifrå dödenom, och föda dem i hårdom tid.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Vår själ väntar efter Herranom; han är vår hjelp och sköld.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
Ty vårt hjerta gläder sig af honom, och vi hoppes på hans helga Namn.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Din godhet, Herre, vare öfver oss, såsom vi på dig förtröste.

< Masalimo 33 >