< Masalimo 33 >
1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Juble, I rettferdige, i Herren! For de opriktige sømmer sig lovsang.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Pris Herren med citar, lovsyng ham til tistrenget harpe!
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Syng en ny sang for ham, spill liflig med frydesang!
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
For Herrens ord er sant, og all hans gjerning er trofast.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
Han elsker rettferdighet og rett; jorden er full av Herrens miskunnhet.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
Himlene er skapt ved Herrens ord, og all deres hær ved hans munns ånde.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Han samler havets vann som en dynge, han legger de dype vann i forrådshus.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
All jorden frykte for Herren, for ham beve alle de som bor på jorderike!
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
For han talte, og det skjedde; han bød, og det stod der.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
Herren omstøter hedningenes råd, han gjør folkenes tanker til intet.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
Herrens råd står fast evindelig, hans hjertes tanker fra slekt til slekt.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Salig er det folk hvis Gud Herren er, det folk han har utvalgt til sin arv.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
Fra himmelen skuer Herren ned han ser alle menneskenes barn.
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
Fra det sted hvor han bor, ser han ned til alle dem som bor på jorden,
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
han som har skapt deres hjerter alle sammen, han som gir akt på alle deres gjerninger.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
En konge frelses ikke ved sin store makt, en helt reddes ikke ved sin store kraft.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
Hesten er ikke å stole på til frelse, og med sin store styrke redder den ikke.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Se, Herrens øie ser til dem som frykter ham, som bier på hans miskunnhet,
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
for å utfri deres sjel fra døden og holde dem i live i hungersnød.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Vår sjel bier på Herren; han er vår hjelp og vårt skjold.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
For i ham fryder vårt hjerte sig, fordi vi setter vår lit til hans hellige navn.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Din miskunnhet, Herre, være over oss, således som vi håper på dig!