< Masalimo 33 >
1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Bino bato ya sembo, bobeta milolo ya esengo na tina na Yawe! Kokumisa Nzambe ebongi na bato oyo bazali alima.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Bosanzola Yawe na nzenze, bosanzola Ye na lindanda ya basinga zomi.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Boyembela Yawe nzembo ya sika, bobetisa bibetelo mindule elongo na koganga ya esengo.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
Pamba te Liloba na Yawe ezali alima, misala na Ye nyonso ekokisamaka na boyengebene.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
Yawe alingaka bosembo mpe alima; mokili etondi na bolingo na Ye.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
Likolo ekelamaki na Liloba na Yawe; mampinga na yango nyonso, na nzela ya pema ya monoko na Ye.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Asangisaka mayi ya bibale minene esika moko, mpe atiaka yango na bisika ya mozindo.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Tika ete mokili mobimba etosa Yawe! Tika ete bavandi nyonso ya mokili balenga liboso na Ye.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
Pamba te alobaki, mpe likambo esalemaki; mpe apesaki mitindo, mpe emonanaki.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
Yawe akweyisaka mikano ya bikolo, abebisaka mabongisi ya bato.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
Kasi mikano ya Yawe etikalaka mpo na seko, mabongisi ya motema na Ye, mpo na bikeke nyonso.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Esengo na ekolo oyo Yawe azali Nzambe na yango. Esengo na bato oyo aponaki mpo na libula na Ye.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
Yawe atalaka wuta na likolo, amonaka bana nyonso ya bato.
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
Wuta na evandelo na Ye, atalaka bavandi nyonso ya mokili.
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
Ye oyo asalaka mitema nyonso ya bato asosolaka makambo nyonso oyo basalaka.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
Ezali te limpinga monene nde ebikisaka mokonzi to nguya monene nde ekangolaka elombe.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
Mpunda ezali na nguya te ya kopesa lobiko, makasi na yango nyonso ekangolaka te.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Nzokande Yawe atalaka bato oyo batosaka Ye, ba-oyo batiaka elikya na bolingo kati na Ye,
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
mpo na kokangola bango na kufa mpe kobatela bango na bomoi ata na tango ya nzala makasi.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Totielaka Yawe motema; azali lisungi mpe nguba na biso.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
Solo, mitema na biso esepelaka kati na Ye, pamba te totiaka elikya na biso kati na Kombo na Ye ya bule.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Yawe, lokola totiaka elikya na biso kati na Yo, tika ete bolingo na Yo ezala elongo na biso.