< Masalimo 33 >

1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Jauchzet dem HERRN, ihr Gerechten! Den Redlichen ziemt Lobgesang.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Preiset den HERRN mit der Harfe, spielet ihm auf dem zehnsaitigen Psalter;
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
singet ihm ein neues Lied, spielet gut, mit Posaunenschall!
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
Denn das Wort des HERRN ist richtig, und all sein Werk ist Treue.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
Er liebt Gerechtigkeit und Gericht; die Erde ist voll der Gnade des HERRN.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
Die Himmel sind durch das Wort des HERRN gemacht und ihr ganzes Heer durch den Geist seines Mundes.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Er türmt die Meereswellen auf und sammelt Wasservorräte an.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Alle Welt fürchte den HERRN, und vor ihm scheue sich alles, was auf dem Erdboden wohnt.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
Denn er sprach, und es geschah; er gebot, und es stand da!
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
Der HERR vereitelt den Rat der Heiden, er verhindert die Anschläge der Völker.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
Der Rat des HERRN besteht ewiglich, seines Herzens Gedanken für und für.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Wohl dem Volk, dessen Gott der HERR ist, dem Volk, das er sich zum Erbe erwählt hat!
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
Vom Himmel schaut der HERR herab, er betrachtet alle Menschenkinder;
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
von seinem festen Thron sieht er alle, die auf Erden wohnen;
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
er, der ihrer aller Herz gebildet hat, bemerkt auch alle ihre Werke.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
Einem König ist nicht geholfen mit viel Heeresmacht, ein Held wird nicht errettet durch große Kraft;
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
das Roß ist unzuverlässig zur Rettung, und trotz seiner großen Stärke kann man nicht entrinnen.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Siehe, der HERR hat ein Auge auf die, so ihn fürchten, die auf seine Gnade hoffen,
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
daß er ihre Seele vom Tode errette und sie in der Teuerung am Leben erhalte.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Unsre Seele harrt auf den HERRN; er ist unsre Hilfe und unser Schild.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
Ja, an ihm soll unser Herz sich freuen; denn auf seinen heiligen Namen haben wir unser Vertrauen gesetzt.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Deine Gnade, o HERR, sei über uns, wie wir es von dir erhoffen!

< Masalimo 33 >