< Masalimo 33 >
1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Justes, exultez dans le Seigneur, aux cœurs droits convient sa louange.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Louez le Seigneur sur la harpe: jouez pour lui du psaltérion à dix cordes.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Chantez-lui un cantique nouveau: par un heureux concert, jouez pour lui du psaltérion, au milieu des acclamations.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
Parce que la parole du Seigneur est droite, et que toutes ses œuvres sont conformes à la fidélité dans les promesses.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
Il aime la miséricorde et la justice: la terre est remplie de sa miséricorde.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
La parole du Seigneur a affermi les cieux: et du souffle de sa bouche, vient toute leur vertu.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Il rassemble comme dans une outre les eaux de la mer: il renferme comme dans des trésors les abîmes.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Que toute la terre craigne le Seigneur: qu’à sa présence aussi soient émus tous ceux qui habitent l’univers.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
Car il a dit, et les choses ont été faites: il a commandé, et elles ont été créées.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
Le Seigneur dissipe les conseils des nations; il réprouve aussi les pensées des peuples, et il réprouve les conseils des princes.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
Mais le conseil du Seigneur demeure éternellement: les pensées de son cœur dans toutes les générations.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Bienheureuse la nation dont le Seigneur est le Dieu! Bienheureux le peuple qu’il a choisi pour son héritage!
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
Du haut du ciel, le Seigneur a regardé: il a vu tous les enfants des hommes.
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
De la demeure qu’il s’est préparée, il a porté ses regards sur tous ceux qui habitent la terre.
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
C’est lui qui a formé un à un leurs cœurs; lui connaît toutes leurs œuvres.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
Un roi ne se sauve point par sa grande puissance, et un géant ne se sauvera point par la grandeur de sa force.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
Le cheval est un espoir trompeur de salut: toute sa force ne le sauvera point.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Voilà que les yeux du Seigneur sont sur ceux qui le craignent, et sur ceux qui espèrent en sa miséricorde,
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
Afin de délivrer leurs âmes de la mort, et de les nourrir dans la famine.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Notre âme attend avec constance le Seigneur, parce qu’il est notre aide et notre protecteur;
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
Parce que c’est en lui que se réjouira notre cœur, et que c’est en son saint nom que nous avons espéré.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Que votre miséricorde, Seigneur, soit sur nous, selon que nous avons espéré en vous