< Masalimo 33 >

1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Entonnez, justes, des chants en l’honneur de l’Eternel: aux hommes droits il sied de louer Dieu!
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Rendez hommage à l’Eternel avec la harpe, célébrez-le par le luth à dix cordes.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Chantez-lui un cantique nouveau, faites résonner avec art vos instruments avec vos acclamations.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
Car droite est la parole de l’Eternel, toute son œuvre est marquée de loyauté.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
Il aime la justice et le bon droit; la terre est remplie de la bonté de l’Eternel.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
Par la parole de l’Eternel les cieux se sont formés, par le souffle de sa bouche, toutes leurs milices.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Il amoncelle comme une digue les eaux de la mer, il renferme dans des réservoirs les flots profonds.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Que toute la terre craigne l’Eternel! Que tous les habitants du globe tremblent devant lui!
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
Car il a parlé, et tout naquit; il a ordonné, et tout fut là.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
L’Eternel renverse les projets des peuples, il fait échouer les desseins des nations.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
Mais les décrets de l’Eternel subsistent à jamais, les résolutions de son cœur, de siècle en siècle.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Heureux le peuple qui reconnaît l’Eternel comme Dieu, la nation qu’il s’est choisie comme son héritage!
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
Du haut des cieux, l’Eternel promène ses regards; il voit tous les fils de l’homme.
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
De la résidence qu’il s’est réservée, il dirige son attention sur tous les habitants de la terre.
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
Il a formé leur cœur à tous, et il observe tous leurs actes.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
Ce n’est pas avec une puissante armée que le roi remporte la victoire; ce n’est pas à sa grande force que le héros doit son salut.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
Le coursier est d’un vain secours pour triompher, et sa grande vigueur n’assure pas le salut.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Voici, les yeux du Seigneur sont ouverts sur ses adorateurs, sur ceux qui ont foi en sa bonté,
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
afin de sauver leur âme du trépas, et de les conserver en vie pendant la famine.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Notre âme met son attente en l’Eternel: il est notre aide et notre bouclier.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
Oui, notre cœur se réjouit en lui, oui, nous avons confiance en son saint nom.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Que ta bonté, Eternel, s’étende sur nous, comme nous y comptons de ta part!

< Masalimo 33 >