< Masalimo 33 >
1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Riemuitkaa Herrassa, te vanhurskaat. Oikeamielisten on soveliasta häntä kiittää.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Ylistäkää Herraa kanteleilla, soittakaa hänelle kymmenkielisillä harpuilla.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Veisatkaa hänelle uusi virsi, helkyttäkää kieliä ihanasti ja riemullisesti.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
Sillä Herran sana on oikea, ja kaikki hänen tekonsa ovat tehdyt uskollisuudessa.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
Hän rakastaa vanhurskautta ja oikeutta; maa on täynnänsä Herran armoa.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
Herran sanalla ovat taivaat tehdyt, ja kaikki niiden joukot hänen suunsa hengellä.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Hän kokoaa meren vedet niinkuin roukkioksi, panee syvyydet säiliöihin.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Peljätköön Herraa kaikki maa, hänen edessänsä vaviskoot kaikki maanpiirin asukkaat.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
Sillä hän sanoi, ja tapahtui niin, hän käski, ja se oli tehty.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
Herra särkee pakanain neuvon, tekee turhiksi kansojen aikeet.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
Mutta Herran neuvo pysyy iankaikkisesti, hänen sydämensä aivoitukset suvusta sukuun.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Autuas se kansa, jonka Jumala Herra on, se kansa, jonka hän on perinnöksensä valinnut!
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
Herra katsoo alas taivaasta, näkee kaikki ihmislapset;
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
asumuksestaan, valtaistuimeltaan hän katselee kaikkia maan asukkaita,
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
hän, joka on luonut kaikkien heidän sydämensä, joka tarkkaa kaikkia heidän tekojansa.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
Ei kuningas voita paljolla väellänsä, ei sankari pelastu suurella voimallansa.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
Turha on sotaratsu auttajaksi, ei pelasta sen suuri väkevyys.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Katso, Herran silmä valvoo niitä, jotka häntä pelkäävät ja panevat toivonsa hänen laupeuteensa,
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
pelastaaksensa heidän sielunsa kuolemasta, elättääksensä heitä nälän aikana.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Meidän sielumme odottaa Herraa, hän on meidän apumme ja kilpemme.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
Sillä hänessä iloitsee meidän sydämemme, me turvaamme hänen pyhään nimeensä.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Sinun armosi, Herra, olkoon meidän päällämme, niinkuin me panemme toivomme sinuun.