< Masalimo 33 >
1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Rejoice in the LORD, O ye righteous, praise is comely for the upright.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Give thanks unto the LORD with harp, sing praises unto Him with the psaltery of ten strings.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Sing unto Him a new song; play skilfully amid shouts of joy.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
For the word of the LORD is upright; and all His work is done in faithfulness.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
He loveth righteousness and justice; the earth is full of the lovingkindness of the LORD.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
By the word of the LORD were the heavens made; and all the host of them by the breath of His mouth.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
He gathereth the waters of the sea together as a heap; He layeth up the deeps in storehouses.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Let all the earth fear the LORD; let all the inhabitants of the world stand in awe of Him.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
For He spoke, and it was; He commanded, and it stood.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
The LORD bringeth the counsel of the nations to nought; He maketh the thoughts of the peoples to be of no effect.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
The counsel of the LORD standeth for ever, the thoughts of His heart to all generations.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Happy is the nation whose God is the LORD; the people whom He hath chosen for His own inheritance.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
The LORD looketh from heaven; He beholdeth all the sons of men;
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
From the place of His habitation He looketh intently upon all the inhabitants of the earth;
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
He that fashioneth the hearts of them all, that considereth all their doings.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
A king is not saved by the multitude of a host; a mighty man is not delivered by great strength.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
A horse is a vain thing for safety; neither doth it afford escape by its great strength.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Behold, the eye of the LORD is toward them that fear Him, toward them that wait for His mercy;
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
To deliver their soul from death, and to keep them alive in famine.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Our soul hath waited for the LORD; He is our help and our shield.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
For in Him doth our heart rejoice, because we have trusted in His holy name.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Let Thy mercy, O LORD, be upon us, according as we have waited for Thee.