< Masalimo 33 >
1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
[A Psalm] of David. Rejoice in the Lord, ye righteous; praise becomes the upright.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Praise the Lord on the harp; platy to him on a psaltery of ten strings.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Sing to him a new song; play skillfully with a loud noise.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
For the word of the Lord is right; and all his works are faithful.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
He loves mercy and judgment; the earth is full the mercy of the Lord.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
By the word of the Lord the heavens were established; and all the host of them by the breath of his [mouth].
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Who gathers the waters of the sea as [in] a bottle; who lays up the deeps in treasuries.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Let all the earth fear the Lord; and let all that dwell in the world be moved because of him.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
For he spoke, and they were made; he commanded, and they were created.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
The Lord frustrates the counsels of the nations; he brings to nought also the reasonings of the peoples, and brings to nought the counsels of princes.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
But the counsel of the Lord endures for ever, the thoughts of his heart from generation to generation.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Blessed is the nation whose God is the Lord; the people whom he has chosen for his own inheritance.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
The Lord looks out of heaven; he beholds all the sons of men.
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
He looks from his prepared habitation on all the dwellers on the earth;
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
who fashioned their hearts alone; who understands all their works.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
A king is not saved by reason of a great host; and a giant shall not be delivered by the greatness of his strength.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
A horse is vain for safety; neither shall he be delivered by the greatness of his power.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Behold, the eyes of the Lord are on them that fear him, those that hope in his mercy;
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
to deliver their souls from death, and to keep them alive in famine.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Our soul waits on the Lord; for he is our helper and defender.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
For our heart shall rejoice in him, and we have hoped in his holy name.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Let thy mercy, O Lord, be upon us, according as we have hoped in thee.