< Masalimo 33 >

1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Rejoice in Jehovah, O ye righteous. Praise is comely for the upright.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Give thanks to Jehovah with the harp. Sing praises to him with the psaltery of ten strings.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Sing to him a new song. Play skillfully with a loud noise.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
For the word of Jehovah is right, and all his work is done in faithfulness.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
He loves righteousness and justice. The earth is full of the loving kindness of Jehovah.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
By the word of Jehovah were the heavens made, and all the host of them by the breath of his mouth.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
He gathers the waters of the sea together as a heap. He lays up the deeps in store-houses.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Let all the earth fear Jehovah. Let all the inhabitants of the world stand in awe of him.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
For he spoke, and it was done. He commanded, and it stood fast.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
Jehovah brings the counsel of the nations to naught. He makes the thoughts of the peoples to be of no effect.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
The counsel of Jehovah stands fast forever, the thoughts of his heart to all generations.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Blessed is the nation whose God is Jehovah, the people whom he has chosen for his own inheritance.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
Jehovah looks from heaven. He beholds all the sons of men.
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
From the place of his habitation he looks forth upon all the inhabitants of the earth;
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
he who fashions the hearts of them all, who considers all their works.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
There is no king saved by the multitude of an army. A mighty man is not delivered by great strength.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
A horse is a vain thing for safety, nor does he deliver any by his great power.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Behold, the eye of Jehovah is upon those who fear him, upon those who hope in his loving kindness,
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
to deliver their soul from death, and to keep them alive in famine.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Our soul has waited for Jehovah. He is our help and our shield.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
For our heart shall rejoice in him because we have trusted in his holy name.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Let thy loving kindness, O Jehovah, be upon us, according as we have hoped in thee.

< Masalimo 33 >