< Masalimo 33 >

1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Veselte se spravedliví v Hospodinu, na upříméť přísluší chválení.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Oslavujte Hospodina na harfě, na loutně, a na nástroji o desíti strunách, žalmy zpívejte jemu.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Zpívejte jemu píseň novou, a huďte dobře a zvučně.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
Nebo pravé jest slovo Hospodinovo, a všeliké dílo jeho stálé.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
Milujeť spravedlnost a soud, milosrdenství Hospodinova plná jest země.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
Slovem Hospodinovým nebesa učiněna jsou, a duchem úst jeho všecko vojsko jejich.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Onť shrnul jako na hromadu vody mořské, a složil na poklad propasti.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Boj se Hospodina všecka země, děstež se před ním všickni obyvatelé okršlku zemského.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
Nebo on řekl, a stalo se, on rozkázal, a postavilo se.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
Hospodin ruší rady národů, a v nic obrací přemyšlování lidská.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
Rada pak Hospodinova na věky trvá, myšlení srdce jeho od národu do pronárodu.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Blahoslavený národ, kteréhož Hospodin jest Bohem jeho, lid ten, kterýž sobě on vyvolil za dědictví.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
Hospodin patře s nebe, vidí všecky syny lidské,
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
Z příbytku trůnu svého dohlédá ke všechněm obyvatelům země.
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
Ten, kterýž stvořil srdce jednoho každého z nich, spatřuje všecky skutky jejich.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
Nebývá král zachován skrze mnohý zástup, ani udatný rek vysvobozen skrze velikou moc svou.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
Oklamavatelný jest kůň k spomožení, aniž ve množství síly své vytrhuje.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Aj, oči Hospodinovy patří na ty, kteříž se ho bojí, a na ty, kteříž očekávají milosrdenství jeho,
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
Aby vyprostil od smrti duše jejich, a živil je v čas hladu.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Duše naše očekává na Hospodina, on jest spomožení naše, a pavéza naše.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
V něm zajisté rozveselí se srdce naše, nebo ve jménu jeho svatém naději skládáme.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Budiž milosrdenství tvé nad námi, Hospodine, jakož naději máme v tobě.

< Masalimo 33 >