< Masalimo 33 >

1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
義人哪,你們應當靠耶和華歡樂; 正直人的讚美是合宜的。
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
你們應當彈琴稱謝耶和華, 用十弦瑟歌頌他。
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
應當向他唱新歌, 彈得巧妙,聲音洪亮。
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
因為耶和華的言語正直; 凡他所做的盡都誠實。
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
他喜愛仁義公平; 遍地滿了耶和華的慈愛。
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
諸天藉耶和華的命而造; 萬象藉他口中的氣而成。
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
他聚集海水如壘, 收藏深洋在庫房。
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
願全地都敬畏耶和華! 願世上的居民都懼怕他!
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
因為他說有,就有, 命立,就立。
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
耶和華使列國的籌算歸於無有, 使眾民的思念無有功效。
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
耶和華的籌算永遠立定; 他心中的思念萬代常存。
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
以耶和華為上帝的,那國是有福的! 他所揀選為自己產業的,那民是有福的!
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
耶和華從天上觀看; 他看見一切的世人。
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
從他的居所往外察看地上一切的居民-
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
他是那造成他們眾人心的, 留意他們一切作為的。
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
君王不能因兵多得勝; 勇士不能因力大得救。
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
靠馬得救是枉然的; 馬也不能因力大救人。
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
耶和華的眼目看顧敬畏他的人 和仰望他慈愛的人,
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
要救他們的命脫離死亡, 並使他們在饑荒中存活。
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
我們的心向來等候耶和華; 他是我們的幫助,我們的盾牌。
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
我們的心必靠他歡喜, 因為我們向來倚靠他的聖名。
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
耶和華啊,求你照着我們所仰望你的, 向我們施行慈愛!

< Masalimo 33 >