< Masalimo 33 >

1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Радвайте се праведници, в Господа; Прилично е за праведните да въздават хваление.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Хвалете Господа с арфа, Псалмопейте Му с десето струнен псалтир.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Пейте му нова песен, Свирете изкусно с възклицание.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
Защото словото на Господа е право, И всичките Му дела са извършени с вярност.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
Той обича правда и правосъдие; Земята е пълна с милосърдието Господно.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
Чрез словото на Господа станаха небесата, И чрез дишането на устата Му цялото им множество.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Той събра като куп морските води, Тури бездните в съкровищници.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Нека се бои от Господа цялата земя; Нека благоговеят с боязън пред Него всички жители на вселената.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
Защото Той каза, и стана; Той заповяда, и затвърди се.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
Господ осуетява намеренията на народите; Прави безполезни мислите на племената.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
Намеренията на Господа стоят твърди до века, Мислите на сърцето Му из род в род.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Блажен оня народ, на когото Бог е Господ, Людете, които е изброил за Свое наследство.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
Господ наднича от небето, Наблюдава всичките човешки чада;
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
От местообиталището Си Гледа на всичките земни жители,
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
Онзи, Който създаде сърцата на всички тях, Който позна всичките им работи.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
Никой цар не се избавя чрез многочислена войска Силен мъж не се отървава с голямо юначество.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
Безполезен е конят за избавление, И чрез голямата си сила не може да избави никого.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Ето, окото на Господа е върху ония, които Ме се боят, Върху ония, които се надяват на Неговата милост,
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
За да избави от смърт душата им, И в глад да ги опази живи.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Душата ни чака Господа; Той е помощ наша и щит наш.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
Защото в Него ще се весели сърцето ни, Понеже на Неговото свето име уповаваме.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Дано да бъде милостта Ти, Господи върху нас Според както сме се надявали на Тебе.

< Masalimo 33 >