< Masalimo 32 >

1 Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
Psalmus David, intelligentia. Beati, quorum remissae sunt iniquitates: et quorum tecta sunt peccata.
2 Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
Beatus vir, cui non imputavit Dominus peccatum, nec est in spiritu eius dolus.
3 Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
Quoniam tacui, inveteraverunt ossa mea, dum clamarem tota die.
4 Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
Quoniam die ac nocte gravata est super me manus tua: conversus sum in aerumna mea, dum configitur spina.
5 Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
Delictum meum cognitum tibi feci: et iniustitiam meam non abscondi. Dixi: Confitebor adversum me iniustitiam meam Domino: et tu remisisti impietatem peccati mei.
6 Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
Pro hac orabit ad te omnis sanctus, in tempore opportuno. Verumtamen in diluvio aquarum multarum, ad eum non approximabunt.
7 Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
Tu es refugium meum a tribulatione, quae circumdedit me: exultatio mea erue me a circumdantibus me.
8 Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
Intellectum tibi dabo, et instruam te in via hac, qua gradieris: firmabo super te oculos meos.
9 Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
Nolite fieri sicut equus et mulus, quibus non est intellectus. In camo et freno maxillas eorum constringe, qui non approximant ad te.
10 Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
Multa flagella peccatoris, sperantem autem in Domino misericordia circumdabit.
11 Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!
Laetamini in Domino et exultate iusti, et gloriamini omnes recti corde.

< Masalimo 32 >