< Masalimo 32 >

1 Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
Maskil de David. Ô! Que bienheureux est celui de qui la transgression est pardonnée, et dont le péché est couvert!
2 Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
Ô que bienheureux est l'homme à qui l'Eternel n'impute point son iniquité, et dans l'esprit duquel il n'y a point de fraude!
3 Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
Quand je me suis tu, mes os se sont consumés; et aussi quand je n'ai fait que rugir tout le jour.
4 Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
Parce que jour et nuit ta main s'appesantissait sur moi, ma vigueur s'est changée en une sécheresse d'Eté. (Sélah)
5 Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
Je t'ai fait connaître mon péché, et je n'ai point caché mon iniquité. J'ai dit: Je ferai confession de mes transgressions à l'Eternel; et tu as ôté la peine de mon péché. (Sélah)
6 Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
C'est pourquoi tout bien-aimé de toi te suppliera au temps qu'on [te] trouve, tellement qu'en un déluge de grandes eaux, elles ne l'atteindront point.
7 Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
Tu es mon asile, tu me gardes de détresse; tu m'environnes de chants de triomphe à cause de la délivrance. (Sélah)
8 Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
Je te rendrai avisé, je t'enseignerai le chemin dans lequel tu dois marcher, et je te guiderai de mon œil.
9 Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
Ne soyez point comme le cheval, ni comme le mulet, qui sont sans intelligence, desquels il faut emmuseler la bouche avec un mors et un frein, de peur qu'ils n'approchent de toi.
10 Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
Plusieurs douleurs atteindront le méchant; mais la gratuité environnera l'homme qui se confie en l'Eternel.
11 Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!
Vous justes, réjouissez-vous en l'Eternel, égayez-vous, et chantez de joie vous tous qui êtes droits de cœur.

< Masalimo 32 >