< Masalimo 32 >

1 Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
Of David a poem how blessed! [is one who] is forgiven of transgression [is one who] is covered of sin.
2 Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
How blessed! [is] a person [whom] not he reckons Yahweh to him iniquity and there not in spirit his [is] deceit.
3 Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
If I kept silent they became worn out bones my in cry of distress my all the day.
4 Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
For - by day and night it was heavy on me hand your it was changed juice my by [the] dry heat of summer (Selah)
5 Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
Sin my I made known to you and iniquity my not I covered I said I will confess on transgressions my to Yahweh and you you forgave [the] guilt of sin my (Selah)
6 Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
On this let him pray every faithful [person] - to you to a time of finding certainly to a flood of waters many to him not they will reach.
7 Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
You - [are] a hiding place of me from distress you will preserve me shouts of deliverance; [surely] you will surround me (Selah)
8 Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
I will instruct you - and I will teach you [the] way which you will go I will counsel [you] [will be] on you eye my.
9 Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
May not you be - like a horse like a mule [which] there not [is] understanding with bridle and halter trapping[s] its to restrain not to draw near to you.
10 Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
Many pains [belong] to wicked [person] and the [one who] trusts in Yahweh covenant loyalty it will surround him.
11 Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!
Rejoice in Yahweh and be glad O righteous [people] and shout for joy O all [people] upright of heart.

< Masalimo 32 >