< Masalimo 32 >
1 Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
A Psalm of David. Maschil. Happy is he whose transgression is forgiven, whose sin is pardoned.
2 Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
Happy is the man unto whom the LORD counteth not iniquity, and in whose spirit there is no guile.
3 Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
When I kept silence, my bones wore away through my groaning all the day long.
4 Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
For day and night Thy hand was heavy upon me; my sap was turned as in the droughts of summer. (Selah)
5 Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
I acknowledged my sin unto Thee, and mine iniquity have I not hid; I said: 'I will make confession concerning my transgressions unto the LORD' — and Thou, Thou forgavest the iniquity of my sin. (Selah)
6 Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
For this let every one that is godly pray unto Thee in a time when Thou mayest be found; surely, when the great waters overflow, they will not reach unto him.
7 Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
Thou art my hiding-place; Thou wilt preserve me from the adversary; with songs of deliverance Thou wilt compass me about. (Selah)
8 Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
'I will instruct thee and teach thee in the way which thou shalt go; I will give counsel, Mine eye being upon thee.'
9 Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
Be ye not as the horse, or as the mule, which have no understanding; whose mouth must be held in with bit and bridle, that they come not near unto thee.
10 Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
Many are the sorrows of the wicked; but he that trusteth in the LORD, mercy compasseth him about.
11 Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!
Be glad in the LORD, and rejoice, ye righteous; and shout for joy, all ye that are upright in heart.