< Masalimo 31 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo; musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi; mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
Dawid dwom. Wo mu, Awurade na manya guankɔbea; mma mʼanim ngu ase; fi wo trenee mu gye me.
2 Tcherani khutu lanu kwa ine, bwerani msanga kudzandilanditsa; mukhale thanthwe langa lothawirapo, linga lolimba kundipulumutsa ine.
Yɛ aso ma me, bra ntɛm begye me; yɛ me bammɔ botan, aban a mʼatamfo nsa renka me.
3 Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa, chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
Sɛ woyɛ me botan ne mʼaban nti, wo din nti di mʼanim na kyerɛ me kwan.
4 Ndimasuleni mu msampha umene anditchera pakuti ndinu pothawirapo panga.
Gye me fi afiri a wɔasum me no mu, efisɛ wo ne me guankɔbea.
5 Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga; womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.
Wo nsam na mede me kra hyɛ; gye me bio, Awurade, Onyankopɔn nokwafo.
6 Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe; ine ndimadalira Yehova.
Mikyi wɔn a wɔsom abosom huhuw; mede me ho to Awurade so.
7 Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu popeza Inu munaona masautso anga ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
Mʼani begye na madi ahurusi wɔ wo dɔ mu, efisɛ wuhu mʼamanehunu, na wunim me kra mu haw.
8 Inu simunandipereke kwa mdani koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.
Womfaa me nhyɛɛ ɔtamfo no nsa mmom wode me nan asisi petee mu.
9 Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto; maso anga akulefuka ndi chisoni, mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
Hu me mmɔbɔ, Awurade, efisɛ me ho yeraw me; awerɛhow ama mʼani so ayɛ kusuu ɔyaw ama me kra ne me honam ayɛ mmerɛw.
10 Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula; mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso, ndipo mafupa anga akulefuka.
Ɔyawdi retew me nkwa so, na abooboo tew me mfe so; ɔhaw nti mʼahoɔden kɔ fam, na me nnompe nso ahodwow.
11 Chifukwa cha adani anga onse, ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga; ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga. Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
Mʼatamfo nyinaa nti, mayɛ ahohora wɔ me nnamfonom mu; nnipa a wonim me suro me, na wɔn a wohu me mmɔnten so guan.
12 Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira; ndakhala ngati mʼphika wosweka.
Obiara werɛ afi me te sɛ nea mawu; mayɛ sɛ kuku a abɔ.
13 Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri; zoopsa zandizungulira mbali zonse; iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane, kuti atenge moyo wanga.
Mete asomsɛm dodow a wɔka ahunahuna atwa me ho ahyia. Wɔrepam me ti so, na wɔbɔ pɔw sɛ wobekum me.
14 Koma ndikudalira Inu Yehova; ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
Nanso mede me ho ato wo so, Awurade; meka se, “Woyɛ me Nyankopɔn.”
15 Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
Me mmere wɔ wo nsam gye me fi mʼatamfo ne wɔn a wɔtaa me no nsam.
16 Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu; pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
Tew wʼanim kyerɛ wo somfo; gye me wɔ wo dɔ a enni huammɔ no mu.
17 Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol )
Mma mʼanim ngu ase, Awurade, efisɛ masu afrɛ wo; mmom, ma amumɔyɛfo anim ngu ase na wɔnna wɔn nna mu komm. (Sheol )
18 Milomo yawo yabodzayo ikhale chete, pakuti chifukwa cha kunyada ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.
Mua atorofo ano, efisɛ wɔde ahantan ne animtiaabu kasa tia atreneefo.
19 Ndi waukulu ubwino wanu umene mwawasungira amene amakuopani, umene mumapereka anthu akuona kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
Wo papayɛ dɔɔso, ɛno na woakora ama wɔn a wosuro wo no ɛno na wode ma wɔn a woguan toa wo no wɔ nnipa anim.
20 Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa, kuwateteza ku ziwembu za anthu; mʼmalo anu okhalamo mumawateteza kwa anthu owatsutsa.
Wode wɔn sie wʼanim bammɔ mu fi nnipa nsusuwii bɔne ho; wo tenabea hɔ na wode wɔn sie dwoodwoo fi tɛkrɛma a ɛbɔ sobo ho.
21 Matamando akhale kwa Yehova, pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
Ayeyi nka Awurade! Sɛ wayi ne dɔ nwonwaso akyerɛ me bere a na mewɔ kuropɔn a atamfo atwa ho ahyia no mu no.
22 Ndili mʼnkhawa zanga ndinati, “Ine ndachotsedwa pamaso panu!” Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.
Mebɔɔ huboa no mekae se: “Woayi wʼani afi me so!” Nanso wotee me mmɔborɔsu bere a mekotow srɛɛ wo no.
23 Kondani Yehova oyera mtima ake onse! Yehova amasunga wokhulupirika koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
Monnɔ Awurade mo a moyɛ nʼahotewfo nyinaa! Awurade kora wɔn a wodi nokware so, na ahomasofo de, otua wɔn ka pɛpɛɛpɛ.
24 Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima, inu nonse amene mumayembekezera Yehova.
Monyɛ den na momma mo bo ntɔ mo yam, mo a mowɔ anidaso wɔ Awurade mu nyinaa.