< Masalimo 31 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo; musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi; mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
Přednímu zpěváku, žalm Davidův. V tebe, Hospodine, doufám, nedejž mi zahanbenu býti na věky, pro spravedlnost svou vysvoboď mne.
2 Tcherani khutu lanu kwa ine, bwerani msanga kudzandilanditsa; mukhale thanthwe langa lothawirapo, linga lolimba kundipulumutsa ine.
Nakloň ke mně ucha svého, rychle vytrhni mne; budiž mi pevnou skalou a domem ohraženým, abys mne zachoval.
3 Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa, chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
Nebo skála má a hrad můj ty jsi, protož pro jméno své veď i doveď mne.
4 Ndimasuleni mu msampha umene anditchera pakuti ndinu pothawirapo panga.
Vyveď mne z leči, kterouž polékli na mne; nebo síla má ty jsi.
5 Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga; womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.
V ruce tvé poroučím ducha svého, nebo jsi mne vykoupil, Hospodine, Bože silný a věrný.
6 Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe; ine ndimadalira Yehova.
Nenávidím těch, kteříž následují pouhých marností, nebo já v Hospodinu naději skládám.
7 Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu popeza Inu munaona masautso anga ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
Plésati a radovati se budu v milosrdenství tvém, že jsi vzezřel na mé trápení, a poznal jsi v ssoužení duši mou.
8 Inu simunandipereke kwa mdani koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.
Aniž jsi mne zavřel v ruce nepřítele, ale postavil jsi na širokosti nohy mé.
9 Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto; maso anga akulefuka ndi chisoni, mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
Smiluj se nade mnou, Hospodine, nebo jsem ssoužen, tak že usvadla zámutkem tvář má, duše má, i život můj.
10 Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula; mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso, ndipo mafupa anga akulefuka.
Žalostí zajisté zhynulo zdraví mé, a léta má od úpění, zemdlena bídou mou síla má, a kosti mé vyprahly.
11 Chifukwa cha adani anga onse, ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga; ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga. Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
U všech nepřátel svých jsem v pohanění, a nejvíce u sousedů, známým pak svým jsem strašidlem; kteříž mne vídají vně, utíkají přede mnou.
12 Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira; ndakhala ngati mʼphika wosweka.
Vyšel jsem z paměti tak, jako mrtvý, učiněn jsem jako nádoba rozražená.
13 Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri; zoopsa zandizungulira mbali zonse; iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane, kuti atenge moyo wanga.
Nebo slýchám utrhání mnohých, strach odevšad, když se proti mně spolu puntují, lstivě přemýšlejíce, jak by odjali duši mou.
14 Koma ndikudalira Inu Yehova; ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
Ale já v tobě naději skládám, Hospodine; řekl jsem: Bůh můj jsi ty.
15 Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
V rukou tvých jsou časové moji, vytrhni mne z ruky nepřátel mých a těch, kteříž mne stihají.
16 Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu; pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
Osvěť tvář svou nad služebníkem svým, zachovej mne pro milosrdenství své.
17 Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol h7585)
Hospodine, ať nejsem zahanben, nebo jsem tě vzýval; nechať jsou zahanbeni bezbožníci, a skroceni v pekle. (Sheol h7585)
18 Milomo yawo yabodzayo ikhale chete, pakuti chifukwa cha kunyada ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.
Oněmějte rtové lživí, kteříž mluví proti spravedlivému tvrdě, pyšně a s potupou.
19 Ndi waukulu ubwino wanu umene mwawasungira amene amakuopani, umene mumapereka anthu akuona kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
Ó jak veliká jest dobrotivost tvá, kterouž jsi odložil těm, jenž se bojí tebe, a kterouž jsi činíval doufajícím v tebe před syny lidskými.
20 Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa, kuwateteza ku ziwembu za anthu; mʼmalo anu okhalamo mumawateteza kwa anthu owatsutsa.
Ty je skrýváš v skrýši oblíčeje svého před vysokomyslností člověka, skrýváš je jako v stanu před jazyky svárlivými.
21 Matamando akhale kwa Yehova, pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
Požehnaný buď Hospodin, nebo prokázal ke mně divné milosrdenství své jako v městě ohraženém.
22 Ndili mʼnkhawa zanga ndinati, “Ine ndachotsedwa pamaso panu!” Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.
Já zajisté když jsem pospíchal, řekl jsem: Zavrženť jsem od očí tvých, ale ty jsi vyslyšel hlas pokorných modliteb mých, když jsem k tobě volal.
23 Kondani Yehova oyera mtima ake onse! Yehova amasunga wokhulupirika koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
Milujtež Hospodina všickni svatí jeho, neboť ostříhá věřících Hospodin, a též odplací vrchovatě tomu, kdož pýchu provodí.
24 Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima, inu nonse amene mumayembekezera Yehova.
Zmužile sobě čiňte, (a posilní Bůh srdce vašeho), všickni, kteříž naději máte v Hospodinu.

< Masalimo 31 >