< Masalimo 30 >
1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
Psalm i pieśń na poświęcenie przybytku Dawida. PANIE, będę cię wywyższać, bo podniosłeś mnie i nie pozwoliłeś mym wrogom cieszyć się z mojego powodu.
2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
PANIE, Boże mój, wołałem do ciebie i uzdrowiłeś mnie.
3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol )
PANIE, wyprowadziłeś moją duszę z piekła, zachowałeś mnie przy życiu, abym nie zstąpił do dołu. (Sheol )
4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
Śpiewajcie PANU, święci jego, i wysławiajcie [go], wspominając jego świętość.
5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
Jego gniew bowiem trwa tylko chwilę, a jego łaskawość przez [całe] życie; choćby płacz trwał przez noc, rankiem nastanie radość.
6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
Powiedziałem w czasie mej pomyślności: Nigdy się nie zachwieję.
7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
PANIE, w swojej łaskawości umocniłeś moją górę; ale gdy ukryłeś swoje oblicze, strwożyłem się.
8 Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
Wołałem do ciebie, PANIE, modliłem się do PANA:
9 “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
Jaki pożytek z mojej krwi, gdybym zstąpił do dołu? Czy proch będzie cię chwalić? Czy będzie głosić twoją prawdę?
10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
Usłysz, PANIE, i zmiłuj się nade mną; PANIE, bądź moim pomocnikiem.
11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
Mój płacz zmieniłeś w taniec, zdjąłeś [ze mnie] wór [pokutny], a przepasałeś mnie radością;
12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.
Aby [moja] chwała śpiewała ci i nie milkła; PANIE, mój Boże, będę cię wysławiać na wieki.