< Masalimo 30 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
Ihubo. Ingoma. Elokunikela ithempeli. ElikaDavida. Ngizakuphakamisa, Oh Thixo, ngoba wangenyula ekujuleni awaze wavumela izitha zami zijabule phezu kwami.
2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
Awu Thixo, Nkulunkulu wami, ngacela Kuwe uncedo wangisilisa.
3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol h7585)
Yebo Thixo wangenyula elibeni, wangisiza ngaphepha ukungena egodini. (Sheol h7585)
4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
Hlabelelani kuThixo lina bathembekileyo bakhe; dumisani ibizo lakhe elingcwele.
5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
Ngoba ukuthukuthela Kwakhe ngokomzuzwana nje, kodwa umusa wakhe ukhona okwempilo yonke; ukulila kungaqhubeka ubusuku bonke, kodwa ukuthokoza kuyafika ekuseni.
6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
Ngathi lapho ngizizwa ngihlezi kuhle ngathi, “Kangisoze ngafa ngahlukuluzeka.”
7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
Yebo Thixo, wathi lapho ungizwela wenza intaba yami yagxila qho; kodwa kwathi lapho usufihle ubuso Bakho ngaphelelwa lithemba.
8 Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
Ngakhala kuwe, Thixo; ngacela umusa eNkosini:
9 “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
“Kulenzuzo bani ngokubhujiswa kwami na, ngokutshona kwami egodini? Kambe uthuli luzakudumisa na? Lona luzafakaza na ngokuthembeka Kwakho?
10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
Zwana, Oh Thixo, ube lomusa kimi; woba lusizo lwami.”
11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
Waguqula ukububula kwami kwaba ngumgido; wangihlubula izigqoko zamasaka wangigqokisa ukuthokoza,
12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.
ukuze inhliziyo yami ikuhlabelele ingathuli. Oh Thixo, Nkulunkulu wami, ngizakubonga nini lanini.

< Masalimo 30 >