< Masalimo 30 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
E HAPAI aku au ia oe, e Iehova, no kou hoopakelo ana ia'u; Aole oe i hoohauoli i ko'u poe enemi maluna iho o'u.
2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
E Iehova ko'u Akua, ua ulono aku au ia oe, A ua hoola mai nei oe ia'u.
3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol h7585)
E Iehova, ua lawe mai oe i kuu uhane mai ka luakupapau: Ua hoomau oe i kuu ola i ole au e iho ilalo i ka lua. (Sheol h7585)
4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
E himeni aku ia Iehova, e kona poe haipule; E hoomaikai hoi i ka hoomanao ana i kona hoano.
5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
No ka mea, hookahi sekona kona huhu: He ola no nae iloko o kona lokomaikai. He uwe ana paha i ka po hookahi; Aka, hiki mai no ka hauoli i ke kakahiaka.
6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
I iho la au i kuu pomaikai ana, Aole loa au e hoonauweweia.
7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
E Iehova, ma kou lokomaikai, ua, hookupaa oe i kuu mauna: Huna aku la oe i kou maka, pilikia iho la au.
8 Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
Kahea aku la au ia oe, e Iehova; Pule aku la hoi au i ka Haku.
9 “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
Heaha ka waiwai o kuu koko i kuu iho ana i ka lua? E hoolea anei ka lepo ia oe? E hai aku anei oia i kou oiaio?
10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
E hoolohe mai, e Iehova, a e aloha mai oe ia'u: E Iehova, e lilo mai oe i kokua no'u.
11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
Ua hoolilo oe i kuu uwe ana i haa ana no'u: Ua kala oe i kuu kapa iuo; A ua kakoo mai oe ia'u me ka hauoli;
12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.
I hoolea ko'u nani ia oe, aole o mumule. E Iehova ko'u Akua, e hoomaikai mau loa aku au ia oe.

< Masalimo 30 >