< Masalimo 30 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
Psaume. Cantique pour la dédicace de la maison. De David. Je t’exalte, ô Éternel, car tu m’as relevé, Tu n’as pas voulu que mes ennemis se réjouissent à mon sujet.
2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
Éternel, mon Dieu! J’ai crié à toi, et tu m’as guéri.
3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol h7585)
Éternel! Tu as fait remonter mon âme du séjour des morts, Tu m’as fait revivre loin de ceux qui descendent dans la fosse. (Sheol h7585)
4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
Chantez à l’Éternel, vous qui l’aimez, Célébrez par vos louanges sa sainteté!
5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
Car sa colère dure un instant, Mais sa grâce toute la vie; Le soir arrivent les pleurs, Et le matin l’allégresse.
6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
Je disais dans ma sécurité: Je ne chancellerai jamais!
7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
Éternel! Par ta grâce tu avais affermi ma montagne… Tu cachas ta face, et je fus troublé.
8 Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
Éternel! J’ai crié à toi, J’ai imploré l’Éternel:
9 “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
Que gagnes-tu à verser mon sang, A me faire descendre dans la fosse? La poussière a-t-elle pour toi des louanges? Raconte-t-elle ta fidélité?
10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
Écoute, Éternel, aie pitié de moi! Éternel, secours-moi!
11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
Et tu as changé mes lamentations en allégresse, Tu as délié mon sac, et tu m’as ceint de joie,
12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.
Afin que mon cœur te chante et ne soit pas muet. Éternel, mon Dieu! Je te louerai toujours.

< Masalimo 30 >