< Masalimo 30 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
A Psalm. A Song for the Dedication of the Temple. By David. I will extol you, LORD, for you have raised me up, and have not made my foes to rejoice over me.
2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
LORD my God, I cried to you, and you have healed me.
3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol h7585)
LORD, you have brought up my soul from Sheol. You have kept me alive, that I should not go down to the pit. (Sheol h7585)
4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
Sing praise to the LORD, you saints of his. Give thanks to his holy name.
5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
For his anger is but for a moment. His favour is for a lifetime. Weeping may stay for the night, but joy comes in the morning.
6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
As for me, I said in my prosperity, “I shall never be moved.”
7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
You, LORD, when you favoured me, made my mountain stand strong; but when you hid your face, I was troubled.
8 Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
I cried to you, LORD. I made supplication to the Lord:
9 “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
“What profit is there in my destruction, if I go down to the pit? Shall the dust praise you? Shall it declare your truth?
10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
Hear, LORD, and have mercy on me. LORD, be my helper.”
11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
You have turned my mourning into dancing for me. You have removed my sackcloth, and clothed me with gladness,
12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.
to the end that my heart may sing praise to you, and not be silent. LORD my God, I will give thanks to you forever!

< Masalimo 30 >