< Masalimo 30 >
1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
A psalm [the] song of [the] dedication of the house of David. I will exalt you O Yahweh for you have drawn up me and not you have allowed to rejoice enemies my to me.
2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
O Yahweh God my I cried for help to you and you healed me.
3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol )
O Yahweh you brought up from Sheol life my you preserved alive me (from going down my *Q(K)*) [the] pit. (Sheol )
4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
Sing praises to Yahweh O faithful [people] his and give thanks to [the] remembrance of holiness his.
5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
For a moment - [is] in anger his life [is] in favor his in the evening it passes [the] night weeping and to the morning a shout of joy.
6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
And I I said in prosperity my not I will be shaken for ever.
7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
O Yahweh in favor your you made stand to mountain my strength you hid face your I was disturbed.
8 Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
To you O Yahweh I called out and to [the] Lord I sought favor.
9 “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
What? [is the] profit in blood my in going down my to [the] pit ¿ will it give thanks to you dust ¿ will it declare faithfulness your.
10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
Hear O Yahweh and show favor to me O Yahweh be a helper of me.
11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
You turned wailing my into dancing to me you loosened sackcloth my and you girded me joy.
12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.
So that - it may sing praises to you honor and not it may be silent O Yahweh God my for ever I will give thanks to you.