< Masalimo 30 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
I will extol you, O LORD; for you have lifted me up, and have not made my foes to rejoice over me.
2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
O LORD my God, I cried unto you, and you have healed me.
3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol h7585)
O LORD, you have brought up my soul from the grave: you have kept me alive, that I should not go down to the pit. (Sheol h7585)
4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
Sing unto the LORD, O all of you saints of his, and give thanks at the remembrance of his holiness.
5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
For his anger endures but a moment; in his favour is life: weeping may endure for a night, but joy comes in the morning.
6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
And in my prosperity I said, I shall never be moved.
7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
LORD, by your favour you have made my mountain to stand strong: you did hide your face, and I was troubled.
8 Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
I cried to you, O LORD; and unto the LORD I made supplication.
9 “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
What profit is there in my blood, when I go down to the pit? Shall the dust praise you? shall it declare your truth?
10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
Hear, O LORD, and have mercy upon me: LORD, be you my helper.
11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
You have turned for me my mourning into dancing: you have put off my sackcloth, and girded me with gladness;
12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.
To the end that my glory may sing praise to you, and not be silent. O LORD my God, I will give thanks unto you for ever.

< Masalimo 30 >