< Masalimo 30 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
A Canticle Psalm. In dedication to the house of David. I will extol you, Lord, for you have sustained me, and you have not allowed my enemies to delight over me.
2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
O Lord my God, I have cried out to you, and you have healed me.
3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol h7585)
Lord, you led my soul away from Hell. You have saved me from those who descend into the pit. (Sheol h7585)
4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
Sing a psalm to the Lord, you his saints, and confess with remembrance of his holiness.
5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
For wrath is in his indignation, and life is in his will. Toward evening, weeping will linger, and toward morning, gladness.
6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
But I have said in my abundance: “I will never be disturbed.”
7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
O Lord, in your will, you made virtue preferable to beauty for me. You turned your face away from me, and I became disturbed.
8 Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
To you, Lord, I will cry out. And I will make supplication to my God.
9 “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
What use would there be in my blood, if I descend into corruption? Will dust confess to you or announce your truth?
10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
The Lord has heard, and he has been merciful to me. The Lord has become my helper.
11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
You have turned my mourning into gladness for me. You have cut off my sackcloth, and you have surrounded me with joy.
12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.
So then, may my glory sing to you, and may I not regret it. O Lord, my God, I will confess to you for eternity.

< Masalimo 30 >