< Masalimo 3 >
1 Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
Davut'un oğlu Avşalom'dan kaçtığı zaman yazdığı mezmur Ya RAB, düşmanlarım ne kadar çoğaldı, Hele bana karşı ayaklananlar!
2 Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
Birçoğu benim için: “Tanrı katında ona kurtuluş yok!” diyor. (Sela)
3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
Ama sen, ya RAB, çevremde kalkansın, Onurum, başımı yukarı kaldıran sensin.
4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
RAB'be seslenirim, Yanıtlar beni kutsal dağından. (Sela)
5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
Yatar uyurum, Uyanır kalkarım, RAB destektir bana.
6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
Korkum yok Çevremi saran binlerce düşmandan.
7 Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
Ya RAB, kalk, ey Tanrım, kurtar beni! Vur bütün düşmanlarımın çenesine, Kır kötülerin dişlerini.
8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)
Kurtuluş RAB'dedir, Halkının üzerinde olsun bereketin! (Sela)