< Masalimo 3 >

1 Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
¡Oh Yavé, cómo se multiplicaron mis opresores! Muchos son los que se levantan contra mí.
2 Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
Muchos dicen de mí: No hay salvación en ʼElohim para él. (Selah)
3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
Pero Tú, oh Yavé, eres escudo alrededor de mí, Mi gloria, y el que levanta mi cabeza.
4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
Clamé a Yavé con mi voz.
5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
Yo me acosté y dormí, Y desperté, porque Yavé me sustenta.
6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
No temeré a decenas de millares de personas Me sitien que alrededor.
7 Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
¡Levántate, oh Yavé, sálvame, ʼElohim mío! Porque Tú eres el que golpea a todos mis enemigos en la mejilla Y quebrantas los dientes de los impíos.
8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)
La salvación corresponde a Yavé. Sobre tu pueblo sea tu bendición. (Selah)

< Masalimo 3 >