< Masalimo 3 >
1 Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
Senhor, como se tem multiplicado os meus adversários! são muitos os que se levantam contra mim.
2 Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
Muitos dizem da minha alma: Não há salvação para ele em Deus (Selah)
3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
Porém tu, Senhor, és um escudo para mim, a minha glória, e o que exalta a minha cabeça.
4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
Com a minha voz clamei ao Senhor, e ouviu-me desde o seu santo monte (Selah)
5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
Eu me deitei e dormi: acordei; porque o Senhor me sustentou.
6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
Não temerei os milhares de povo que se puseram contra mim e me cercam.
7 Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
Levanta-te, Senhor; salva-me, Deus meu; pois feriste a todos os meus inimigos nos queixos; quebraste os dentes aos ímpios.
8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)
A salvação vem do Senhor; sobre o teu povo seja a tua benção. (Selah)