< Masalimo 3 >

1 Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
Salmo di Davide quando fuggiva il figlio Assalonne. Signore, quanti sono i miei oppressori! Molti contro di me insorgono.
2 Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
Molti di me vanno dicendo: «Neppure Dio lo salva!».
3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
Ma tu, Signore, sei mia difesa, tu sei mia gloria e sollevi il mio capo.
4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
Al Signore innalzo la mia voce e mi risponde dal suo monte santo.
5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
Io mi corico e mi addormento, mi sveglio perché il Signore mi sostiene.
6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
Non temo la moltitudine di genti che contro di me si accampano.
7 Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
Sorgi, Signore, salvami, Dio mio. Hai colpito sulla guancia i miei nemici, hai spezzato i denti ai peccatori.
8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)
Del Signore è la salvezza: sul tuo popolo la tua benedizione.

< Masalimo 3 >